"MWINA SITIMATHA KUSIYANITSA ZIKHO ZINA NDI LIGI" - KALINDA
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Kamuzu Barracks, Ted Kalinda, wati timu yake yakanika kuchita bwino mu zikho zina za mdziko muno kusiyana ndi ligi chifukwa choti masewero onse amawasewera mofanana.
Iye amayankhula atatha masewero omwe agonja 3-1 ndi Blue Eagles lachinayi kuti atuluke mu chikho cha Castel Challenge Cup ndipo iye anati timuyi sinasewere bwino ndipo imayeneradi kugonja ndi kaseweredwe kameneko.
Iye wati timuyi yavutika kuti ichite bwino mu zikho zina monga FDH Bank, Airtel Top 8 komanso cha Castel kamba ka kaganizidwe ka mmene azisewerera masewerowa.
"Ndi zoona kuti tavutikadi mma cup bolako mu ligi mwina chifukwa cha kaganizidwe chifukwa amu zikho zinazi timasewera kuti zithere pomwepo pomwe mu ligi kufanana mphamvu mmasewero enawo timadzapambana nde kusasiyanitsaku ndi komwe kwatipweteketsa." Anatero Kalinda.
Timu ya KB ili pa nambala yachinayi mu ligi ya TNM ndi mapointsi 45 pa masewero 29 omwe yasewer
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores