"ZA FDH TAYIWALA TIKUYANG'ANA ZIKHO ZINA" - MUNTHALI
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya FCB Nyasa Big Bullets, Heston Munthali, wayamikira anyamata ake kamba kosewera bwino mpaka kutetezanso chikho cha FDH Bank masana a lamulungu.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe anapha MAFCO 3-0 kuti atenge chikhochi koma iye wati maso awo tsopano aika pa zikho zina tsopano.
"Mmene zateremu ndekuti za FDH zatha apa tikuyang'anani masewero omwe akubwera kutsogoloku, inde alipo ambiri nde tiyamba kukonzekera mawa ndipo anyamata onse akonzekere kugwira ntchito." Anatero Munthali.
Timuyi yalandira ndalama zokwana K30 million kamba kokhala akatswiri a mpikisanowu omwe tsopano awutenga kachiwiri motsatana.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores