"NGAKHALE DEDZA YACHITA KUTI TINAKUMANA NAZO" - KANANJI.
Mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Eliya Kananji, wati timu yake inasewera bwino kwambiri koma zavuta ndi kukanika kugoletsa ndi chifukwa chake agonja masewero awo 2-1 ndi Dedza Dynamos.
Iye amayankhula izi atatha masewerowa ndipo wati timu yake ndi imene inasewera bwino kuposa Dedza Dynamos koma chibwana cha osewera chawapweteketsa.
"Anali masewero abwino kwambiri anyamata analimbikira koma tizibwana pang'ono ta anyamatawa ndi timene tatipweteketsa, anzathuwa anangobwera ndi kutichinya koma tinawapanikiza ndithu ndipo akuchita kunena okha kuti lero anakumana nazo." Anatero Kananji.
Iye wati kutaya mapointsi kukupereka ntchito yaikulu koma mavuto awo awakonza. Blue Eagles ikadali pa nambala 10 ndi mapointsi 30 pa masewero 25 omwe yasewera.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores