BULLETS IKUYANG'ANA KUTSOGOLO
Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yayankhulapo pa zifukwa zomwe akusewerera masewero a mu TNM Supa ligi ngakhale ali ndi osewera anayi ku Flames komanso ena ambiri ovulala ponena kuti akuyang'ana kutsogolo kwa iwo poti akutenga nawo mbali mu mipikisano yambiri.
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu, Heston Munthali ndiyemwe anayankhula izi patsogolo pa masewero awo ndi timu ya Blue Eagles lamulungu pa bwalo la Kamuzu. Iye wati iwo sakuyang'ana yamatimu ena koma iwo akupanga za Bullets basi.
"Tikumenya masewero ngati Bullets, tili ndi mipikisano yambiri yomwe tisewere nde ife tikuona kumbali yathu, enawonso adzaseweranso masewero awo koma kwa ife tikuyang'ana zomwe zili kutsogolo kwathu." Anatero Munthali.
Pa masewero awo ndi Blue Eagles, iye wati wawauza anyamata kuti akagwiritse ntchito mipata yomwe ikapezeke ndipo wati kumbali ya zigoli, ziyamba kupezeka.
"Ndikukhulupilira kuti anyamata ake ndi omwewa omwe amatipezera zigoli mmbuyomu nde zipezekanso kutsogolo
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores