KAYIRA WACHOKA KU LIBERTY
Mphunzitsi watimu ya Liberty FC, Chimango Kayira, walengeza kuti watula pansi pa udindo wake.
Iye wati wapanga chiganizochi kamba koti samagwira ntchito yake mwa ufulu kamba koti ena amalowerera pa ntchito ndi ziganizo zake.
Iye wati ndi wokondwa kuti wathandizira timuyi mochuluka komanso kuti anabweretsa ndi kuthandizira osewera mu kaseweredwe kawo ndipi wathokoza akuluakulu a timuyi.
Wosewera wakale wa FCB Nyasa Big Bullets, ESCOM United komanso timu ya dziko linoyu sanafotokoze chitsogolo cha ntchito yake.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores