Mtsogoleri wa Malawi Local Government Association, Isaac Jomo Osman, wati bungwe la Football Association of Malawi lipepese pasanathe maola 24 pa zomwe zinachitikira mfumu ya mzinda wa Lilongwe, a Peter Banda.
A Banda analetsedwa kukapereka nawo mphoto kwa osewera amatimu a Mighty Wanderers komanso FCB Nyasa Big Bullets pomwe masewero amu Charity Shield anatha.
A Osman ndi achiwiri kuyankhulapo pa nkhaniyi pomwe unduna wa zamasewero watulutsa kale kalata koma khonsolo ya mzinda wa Lilongwe sinayankhule kalikonse.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores