"NDAWAUZA KUTI ATIPEZERE ENA" - CHIRWA
Mphunzitsi yemwe walembedwa kumene kumbali ya timu ya FOMO, Gilbert Chirwa, walonjeza timuyi kuti ichita bwino kwambiri mu chikho cha Supa ligi ndipo wawauza eni ake kuti amupezere osewera atsopano.
Iye amayankhula pomwe amalandilidwa kutimuyi atasaina mgwirizano wa chaka chimodzi nditimuyi yomwe yangolowa kumene kuchokera mu ligi yachigawo chakummwera yomwe anapambana atagonjetsa Ntopwa.
Chirwa, yemwe chaka chatha amaphunzitsa ku Dedza Dynamos, wati wapempha mkulu watimuyi kuti ayesetse kumupezera osewera ena atsopano kuti alimbitse timuyi.
"Pa zokambirana zathu ndinawapempha kuti mwina atipezere osewera ena atsopano kuti alumikizane ndi ena omwe alowetsa timuyi mu Supa ligi, ndikukhulupilira kuti choncho zithandiza kuti timu izichita bwino." Iye anatero.
Iye anatinso kutimu iliyonse yomwe amapita amachita bwino ndipo akuyembekezera kuti ku FOMO zichitanso chimodzimodzi ndipo ikamatha chakachi idzakhala yatsala mu ligiyi. Kumbali ya omuthand
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores