"SITILI PA MTENDERE NDIPO TIKUFUNIKA KUCHILIMIKA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati ndi wokondwa kwambiri kamba koti timu yake yapeza chipambano pomwe amasewera ndi Civo United koma wati sizikutanthauza kuti ali pa mtendere.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe apambana 1-0 pa bwalo la Rumphi ndipo wati samayembekezera kuti timuyi ingasewere bwino motero.
"Ndine wosangalala kwambiri Chimwemwe chodzadza tsaya komanso ndiwanyadire osewera athu sindimayembekezera kuti tingapambane poti anyamata ambiri ndi ovulala koma asewera bwino. Tichilimikabe chifukwa ligi yavuta nde pakufunika osamataya mapointsi." Anatero Chingoka.
Moyale tsopano yafika pa nambala 11 pomwe yatolera mapointsi 29 pa masewero 23 omwe yasewera mu ligiyi.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores