BREAKING
Timu ya Moyale Barracks yaimitsa ntchito mphunzitsi, Nicolas Mhango, kamba ka kusachita bwino kwa timuyi.
Izi zadziwika pa mkumano umene timuyi inali nawo yowunikira mmene timuyi ikuchitira komanso zifukwa zimene isakuchitira bwino.
Padakali pano, Victor Chingoka, yemwe ndi wachiwiri kwa Mhango, atsogolera timuyi pomwe ikukumana ndi Extreme FC loweruka pa bwalo la Nankhaka.
Mhango anatulutsa kale Bangwe All Stars mu chigawo choyamba ndipo ili pa nambala yachisanu ndi chiwiri (7) pomwe Moyale ili pa nambala 14 ndi mapointsi 23.
Source: VOL
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores