CIVO YAPEZA UBALE NDI KAMPANI YA TREE BUSINESS SUPPLY
Timu ya Civo United yapalana ubwenzi ndi kampani ya Tree Business Suppliers Malawi Limited partners omwe asainirana mgwirizano wa zaka ziwiri kuyambira mu ligi ya chaka cha mawa.
Timuyi yalengeza za mgwirizanowu lachinayi atagwirizana za mgwirizanowu womwe timu ya Civo ithandize kutsatsa malonda a kampaniyi pomwe zovala za Civo zizilembedwa dzina la kampaniyi uku ikuthandiza kugula unifolomu, majuzi, zikwana ndi zina zambiri.
Kampaniyi yati thandizo lawo lizifikiranso ku matimu achisodzera atimuyi komanso timu ya mpira wamiyendo koma ali amayi yatimuyi pofuna kuonetsa kukhazikika kwao pa thandizoli.
Mbali zonse ziwiri zati ndi zosangalala ndi mgwirizanowu womwe uthandize kutukula ntchito za mbali zonse komanso kulumikizitsa ochemerera ndi makasitomala a kampaniyi.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores