CIVO ILI NDI MKUMANO LACHITATU
Timu ya Civo United ikhala ndi mkumano lachitatu kuti ikaunikire za mmene timuyi isakuchitira bwino kutsatira kupezeka kumunsi kwa ligi ya chaka chino.
Mlembi wamkulu watimuyi, Edgar Chilipanjira, watsimikiza za nkhaniyi pomwe wati akufuna kufufuza chimene chikuchititsa kuti timuyi isamachite bwino mmasewero awo.
Izi zabwera kutsatira kugonja masewero atatu otsatizana ndipo ali pa nambala yachikhumi ndi chitatu (13) pomwe yatolera mapointsi 24 pa masewero 21.
Mkumanowu ukhudza akuluakulu atimuyi, aphunzitsi komanso osewera atimuyi ndipo a Chilipanjira akukhulupilira kuti izi zithandiza kuyambiranso kuchita bwino.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores