"NDINANENA KALE KUTI BLUE EAGLES SINGATULUKE" - KANANJI
Mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Eliya Kananji, watsindika kuti timu yawo singatuluke mu ligi ya TNM ndipo anthu ayionanso ikusewera momwemu chaka cha mawa.
Kananji amayankhula izi atatha masewero omwe apambana 1-0 ndi Civo ku bwalo la Champions ndipo wati masewero anali ovuta koma chigoli cha msanga chawathandiza. Iye wati anyamata ake tsopano akubweramo pa mmene amafunira.
"Chichitikireni mkumano wathu uja, tapambani iyiyi yachiwiri ndipo tafanana mphamvu imodzi zomwe zikusonyeza kuti anyamata akubweramo ndipo tichita bwino. Ndinanena kale kuti nzosatheka kuti timu yathu ikhonza kutuluka mu ligi." Anafotokoza Kananji.
Timu ya Blue Eagles ili pa nambala yachikhumi ndi chiwiri (12) pomwe yatolera mapointsi okwana 24 pa masewero 21 omwe asewera.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores