KUSINTHA KUKUONEKA KU EAGLES
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Christopher Sibale, wati timu yake yayamba kuonetsa kusintha pomwe ayamba kutolera mapointsi mmasewero omwe asewera posachedwa.
Eagles inagonjetsa Mighty Wakawaka Tigers ndipo yafanana mphamvu mmasewero awo sabata yatha ndipo patsogolo pa masewero awo ndi Civo United pa bwalo la Champions ku Dowa, Sibale wati akonzeka.
"Tinafika mu Lilongwe ndipo tayamba kukonzekera masewero ndi Civo, zikuoneka kuti zinthu zayamba kuyenda ndipo zitati zipitilire ndekuti tikhonza kuchoka kumunsi kumene tili kuja." Anatero Sibale.
Timu ya Blue Eagles ikadali ku chigwa cha matimu otuluka mu ligi pomwe ili pa nambala 14 ndi mapointsi 21 pa masewero 20.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores