NGINDE WATI CHITIPA SINATOPE
Mphunzitsi watimu ya Chitipa United, MacDonald Mtetemera, wati timu yake sikuti yatopa koma masewero akoyenda amakhala ovuta kwambiri kwa matimu osiyanasiyana.
Nginde wayankhula izi patsogolo pa masewero awo ndi timu ya Bangwe All Stars pomwe wati timu yake yakonzekera bwino masewerowa ndipo ikuyang'ana za chipambano mtsiku la lero.
"Anyamata akonzekera za kugonja ndi Tigers aziyiwala awa ndi masewero ena omwe tikuyenera kuikapo mtima kuti tipambane. Sikuti anyamata atopa ayi, komano tikayenda mwina zimavuta kuti tipeze zipambano nde koma tikulimbikirabe kuti tizichita bwino." Anatero Mtetemera.
Timuyi ikapambana masewerowa itsogolera ndandanda wa matimu 16 mu ligi ya TNM koma ikhala kuti yasewera masewero ochuluka kusiyana ndi omwe akupikisana nawo. Chitipa ili pa nambala yachitatu ndi mapointsi 36.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores