"OYIMBIRA AKUMATENGA MBALI PA MASEWERO" - KANANJI
Mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Eliya Kananji, wati oyimbira mmasewero awo ndi Karonga United anatenga gawo lina lolepheretsa kuti apambane koma kutenga point imodzi koyenda ndi chamuna.
Kananji amayankhula izi atatha masewerowa omwe matimuwa analepherana 0-0 pa bwalo la Karonga ndipo wayamikira osewera ake kamba kozipereka mmasewerowa.
"Tithokoze Mulungu kuti tasewera ndi Karonga United, tiwayamikirenso anyamata athu agwira ntchito yotamandika, tinabwera ndipo tinayesetsa kuti mwina tipeze chipambano komabe achina Newton akumatenga mbalinso yaikulu bola asamakhale ndi mbali." Kananji anafotokoza.
Iye wati point yomwe atenga mmasewerowa iwathandize kupita patsogolo ndipo wati pang'onopang'ono akhale akuyendabe kuthawa chigwa cha matimu otuluka. Eagles yafika pa nambala 13 ndi mapointsi 21 mmasewero 20.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores