Timu ya Masters FC yatsimikiza kuti itenga nawo mbali mu mpikisano wa Mwini Mzinda Charity omwe akupangitsa ndi mfumu ya mzinda wa Lilongwe.
Masewerowa adzaseweredwa pa bwalo la Bingu kuyambira pa 11 mpaka pa 12 April 2026.
Mpikisanowu ukhala wa matimu anayi omwe kupatula Masters, palinso Silver Strikers, Civil Service United ndi Creck Sporting Club.
Masewerowa agwira ntchito kuti apeze ndalama zothandizira kukonza ukhondo wa mzindawu komanso matimu akonzekera ligi ya chaka cha 2026.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores