WANDERERS YAMVANA NDI MADINGA
Katswiri wa Flames, Francisco Madinga, tsopano akuyembekeza kusaina mgwirizano wake ndi timu ya Mighty Mukuru Wanderers pomwe mbali zonse ziwiri tsopano zamvana pa zimene akufuna.
Madinga anabwera mdziko muno atathetsa mgwirizano wake ndi timu yaku Botswana ya Jwaneng Galaxy kamba kosowa mpata osewera ndipo anapita ku Amazulu kukayesa mwai komwe sizinatheke.
Iye anayamba zokonzekera ndi timuyi pomwe amakambirana Kaye kamba koti amafuna kusaina mgwirizano wa chaka chimodzi koma Wanderers imakana.
Nkhani yamveka tsopano kuti mbali zonse zamvana chimodzi ndipo Madinga awoneka ku Manoma mchigawo chachiwiri pomwe akhale akusaina mgwirizano wake.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores