WANDERERS IKUFUNA AARON
Timu ya Mighty Mukuru Wanderers ikuyembekezeka kupereka pempho la ndalama kutimu ya Civo United kuti itenge katswiri wawo wapakati, Lloyd Aaron, kuti apite kutimuyi.
Malipoti akuonetsa kuti timuyi sinafikire Civo koma ikukonza zotero kuti alimbitse timu yawo mchigawo chachiwiri.
Aaron wadziwika kwambiri ku mpikisano wa COSAFA pomwe anasewera mwapamwamba ndi timu ya Flames. Manoma ali pa nambala yachinayi mu ligi ya TNM pomwe yatolera mapointsi 28 pa masewero 15.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores