MADINGA WABWERERA KU WANDERERS
Katswiri wa Flames, Francisco Madinga, wayamba zokonzekera ndi timu ya Mighty Mukuru Wanderers pomwe akuchita zokambirana kuti abwererenso ku timuyi.
Madinga anachoka mu 2022 pomwe anapita kutimuyi ya Dila Gori FC yaku Georgia komwe wasewerako chaka chimodzi ndipo anapitanso ku Jwaneng Galaxy yaku Botswana ndipo anapambanakonso chikho komabe wachoka kamba kosasewerasewera.
Iye anakayesanso mwayi ku timu ya Amazulu mwezi wathawu komabe wakanika kusaina mgwirizano ndi timuyi. Iye tsopano akuyembekezeka kuthandiza timuyi mu chigawo chachiwiri cha ligi ya TNM.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores