BANGWE WATENGA KAMWENDO
Timu ya Bangwe All Stars, yatenga mphunzitsi watimu ya Mighty Wanderers Youth, Joseph Kamwendo, kuti akakhale wogwirizira pomwe akuyang'anabe mphunzitsi okhazikika.
Timuyi yalengeza za nkhaniyi lachiwiri molingana ndi mmene ankalengezera akumutsitsa udindo Mavuto Lungu kupita ku timu yaying'ono yawo.
Kamwendo athandizidwa ndi Joseph Semu Ndipo Dave Pashane akhale mphunzitsi wama Goloboyi watsopano pomwe Steve Madeira akhalebe Technical Manager.
Kamwendo sangamutengeretu kukhala mphunzitsi poti ali ndi chiphaso chauphunzitsi cha CAF C koma bungwe la Super League of Malawi limafuna aphunzitsi ayambire kukhala ndi CAF B ndi CAF A.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores