NYAMBOSE AKANALI NDI TIGERS
Mphunzitsi watimu ya Mighty Wakawaka Tigers, Christopher Nyambose, akadali ndi timuyi ngakhale kuti timuyi inalengeza kuti yamuchotsa ntchito kamba kosachita bwino.
Mphunzitsiyu anatsogolera timuyi mmasewero omwe analepherana 0-0 ndi timu ya Blue Eagles loweruka ndipo anabwerera ku zokonzekera patangotha tsiku limodzi chimuchotsereni.
Iye akuyembekeza kutsogolera timuyi mmasewero awo omaliza a ligi pomwe akumane ndi FCB Nyasa Big Bullets lachitatu.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores