MPULULA ALENGEZEDWA KU TIGERS
Timu ya Mighty Wakawaka Tigers yatsala pang'ono kumalizitsa zotenga mphunzitsi yemwe wachoka ku Silver Strikers, Leo Mpulula, kuti atsogolere timuyi mu chaka cha 2024.
Izi ndi malingana ndi zomwe tapeza kuti ligi ya chaka chatha itangotha, akuluakulu a timuyi anamupeza mphunzitsiyu kuti atsogolere timuyi ndi chifukwa chake anatsanzika ku Silver.
Mpulula akuyembekezeka kulengezedwa tsiku lililonse mu sabata yomwe ino kukhala mlowammalo wa Christopher Nyambose kutimuyi.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores