"TIGWIRITSA NTCHITO MWAYI WOSEWERA PAKHOMO" - SIBALE
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Christopher Sibale, wati masewero awo ndi Mighty Mukuru Wanderers lachitatu likudzali pa bwalo la Nankhaka akhala ovuta koma iwo agwiritsa ntchito mwayi wosewera pakhomo.
Iye amayankhula izi patsogolo pa masewerowa ndipo wati masewerowa akhala ovuta ndipo atapambana masewero anayi otsogozana, iye wati osewera asazitenge kuti afikapo.
"Ndi masewero ovuta kwambiri koma zitengera kuti ifeyo takonzeka motani ndipo tikufunikira chipambano kuti tipitilire kukwerabe kumtunda kuja nde anyamata akonzeka kwambiri. Ifeyo takonzeka koma kwambiri tigwiritsa ntchito mwayi wa pakhomo, tili pakhomo nde tikufunikira chipambano." Anatero Sibale.
Blue Eagles ikapambana masewerowa ifika pa nambala yachisanu ndi chimodzi (6) pomwe padakali pano ali ndi mapointsi 30 pa masewero 23 omwe yasewera mu ligiyi.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores