FLAMES SISEWERA NAWO CHAN
Bungwe loyendetsa mpira mdziko muno, Football Association of Malawi, lalengeza kuti timu ya dziko lino sisewera nawo masewero amu chikho cha CHAN cha chaka cha 2024.
Bungweli lanena izi ati kamba koti alibe ndalama zokwana zomwe zingawatheketse kuti atenge nawo mbali mu mpikisanowu.
Osewera omwe amasewera mmaligi a mdziko momwemo ndi omwe amaloledwa kusewera mu chikhochi.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores