KANANJI NDI OSEWERA AKE ATSEGULIRIDWA MILANDU
Bungwe la Super league of Malawi (Sulom) latsegulira mlandu ena mwa akuluakulu komanso osewera atimu ya Blue Eagles kamba konyazitsa masewero ampira wamiyendo pomwe timuyi imasewera ndi Ekwendeni Hammers pa 2 July 2023 pabwalo la Mzuzu.
Pamasewerowa anthuwa sanakhutire ndimomwe Oyimbira Rose Zimba, Pierre Kumwenda,Khumbo Madhlopa komanso Mike Misinjo posakhutira ndimomwe anagwilira ntchito zomwe zinapangitsa kuti awathamangitse pamapeto pa masewerowo.
Anthu omwe Sulom yatchula kuti ayankhe mlandu ndimonga:
Eliya Kananji Christopher Sibale Chimwemwe Chitedze Schumacher Kuwali Micium Mhone Tonic Viyuyi Lanken Mwale Chakonda Majanga Richard Lapson
Ngati anthuwa apezeke olakwa akhale akupatsidwa chilango
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores