Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yaika katswiri wawo wakale, Fischer Kondowe, kukhala wachiwiri kwa mphunzitsi watimu pomwe alowe mmalo mwa Peter Mponda.
Kondowe wakhala akugwira ntchito ngati mmodzi mwa aphunzitsi kutimuyi koma wakwera udindo kamba kochoka kwa Mponda.
Peter Mponda anachoka kutimuyi pomwe anapeza ntchito ngati wachiwiri kwa mphunzitsi kutimu ya Black Leopards ku South Africa.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores