Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
KUSINTHA KWA NDONDOMEKO YA MPIKISANO WOLOSERA PA OWINNA.
Tikulengeza za kusintha kwa mpikisano wosolera pa Owinna mnjira zitatu motere:
1. Olandira mphoto akhala omwe afika kapena kudutsa pa nambala 4 pa mndandanda wa olosera molondola, kusiyana ndi mmbuyomu pomwe amalandira ndi omwe afika kapena kudutsa pa nambala 2. Izi ziyambira amene apambane sabata ino omwe adziwike Lolemba pa 17 Feb 2025.
2. Mphoto imene olosera molondola amagawana sabata iliyonse ikwera kuchoka pa MK30,000 kufika pa MK40,000. Izinso ziyambira omwe apambane sabata ino.
3. Usiku walero, tiyamba kubisa zigoli zomwe ena alosera gemu isanayambe. Olosera adziona zigoli zawo zokha pomwe za ena idzingolemba "Prediction *-*" basi. Tidzionetsanso momwe anthu ambiri aloserera poonetsa nambala yanthu omwe aloserera mofanana.
Zabwino zonse pamene tikupitiriza kunyadira akatswiri odziwa kulosera!
Tumizilani Ku 0991509953
Chisankho chakumpoto chaimitsidwa
Chisankho chomwe chimachitika ku bungwe loyendetsa mpira mchigawo chakumpoto chasunthidwa tsiku kamba koti opambana pa mpando wa wapampando ku bungweli samapezeka.
Wapampando yemwe anali ku bungweli, Chauka Mwasinga, amapikisana ndi mlembi wamkulu, Masiya Nyasulu pa mpandowu koma kawiri konse iwo apeza mavoti 13-13.
Malingana ndi uthenga womwe walembedwa pa tsamba la mchezo la Facebook la bungweli, chisankhochi sichipitilira ndipo masiku atsopano alengezedwa mtsogolomu.
Ilo lati bungwe la Football Association of Malawi ndi limene lipereke chitsogozo cha mmene zisankhozi zichitikire kutsogoloku.
Ngakhale zili chomwechi, maudindo omwe amagwira kwa zaka zinayi zapitazi kufikira mu tsiku la lero akhalabe asali mmanja mwa adindo akalewa.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
Demakude: Chimwemwe changa ndi chachikulu
Katswiri yemwe wasaina mgwirizano wake ndi Silver Strikers, Felix Demakude, wati akuyembekezera kuti kaseweredwe kake kasintha kwambiri poti akumana ndi osewera ena omwe amuthandizenso kwambiri.
Iye amayankhula atasaina mgwirizano wa zaka zitatu ndi timuyi pomwe wapitako mwaulere ndipo wati ndi okondwa popita imodzi mwa matimu akuluakulu mdziko muno.
Iye anati: "Ndikukhulupilira kuti kaseweredwe kanga kasintha chifukwa kulinso anzanga omwe amapita ku Flames nde tikhale tikuthandizana kupititsa timu patsogolo." Iye anafotokoza.
Demakude amasewera timu ya Bangwe All Stars chaka chatha koma waphunzira kwambiri mpira wake ku FCB Nyasa Big Bullets Reserve.
Iye wakhala osewera wachitatu kusaina ndi timu ya Silver Strikers chaka chino pomwe yasainako Sam Adeyemi komanso Festus Duwe.
Wanderers at risk of losing another defender
As Mighty Wanderers supporters believe that they need to add defenders, the team is at risk of losing Ahamad Kung'unde who is yet to start pre-season training with the team.
Full story:
Kung'unde was promoted to the senior team from the Reserve side in 2022 and was used as a back up in the defense.
Meanwhile, towards the end of last season, he asked the team's board to hike his salary as he is the only regular receiving a small package.
However, nothing has been done on the issue forcing the player not start trainings with the team.
According to the player, he is very ready to leave the team if nothing changes.
Some members of the technical panel are trying to convince the bosses to do the demands of the player to avoid losing him but some bosses want him leave the team.
Some members of the technical panel are trying to convince the bosses to do the demands of the player to avoid losing him but some of the bosses are ignoring it.
Chigoga: Munthali has a vast experience
FCB Nyasa Big Bullets Chief Executive Officer, Mr Albert Chigoga, says the team settled for Heston Munthali to lead their Reserve side because he has a vast experience with the Senior team in the past 7 years.
He said this as Munthali was confirmed as a head coach for the Reserve side replacing Enos Chatama who left the team after 9 years.
He said he hopes Munthali will do a very good job to produce players for the senior team.
"Coach Hes [Heston Munthali] came here in 2017 when he had just FAM C coaching license but we have developed him and has now a CAF B so we have trusted him because he was with the senior team as a assistant coach and striker's trainer and that experience we hope will help the team." Said Chigoga.
Meanwhile, speaking after given the position, Munthali believes with cooperation, they will do a great job.
"I am very happy to have this job. Our job is to produce players for the Senior team, if we work well with some guys
NKHOMA TO JOIN RED ARROWS
Malawian forward, Zeliat Nkhoma, is currently in Lusaka, Zambia where is set to join Zambian military side and MTN Super League defending champions, Red Arrows FC.
According to reports in Zambia, Nkhoma, who played for Flames last year will be confirmed as a Arrows player soon.
Arrows was on the market looking for a striker after the departure of their deadly forward, Ricky Banda last month.
Nkhoma plays for 2016 TNM Super League Champions, Kamuzu Barracks and scored 15 goals last season in all competitions and one at Flames in 2024.
NEWS
FCB Nyasa Big Bullets has announced that Heston Munthali Kajore will be the head coach for their Reserve team.
The team made the announcement on thursday through their Facebook page.
Munthali, who in the past years served as a deputy coach of Kalisto Pasuwa at the senior team, replaced Enos Chatama who left the team for Ekhaya FC.
Haiya: Tabitha, Temwa ndi akunja onse abwera
Mtsogoleri wa bungwe loyendetsa mpira mdziko muno la Football Association of Malawi, Fleetwood Haiya, wati timu ya Scorchers ikhale ndi osewera ake onse omwe imadalira.
Iye amayankhula lachitatu pa mwambo omwe bungweli limayankhula pa zinthu zosiyanasiyana ku Chiwembe ndipo amatsimikiza kuti ulendo waku Zambia ulipo.
Iye wati Zambia ikhale ikutenganso timu yawo yonse yomwe amadalira chomwechonso Malawi itero.
"Achina Tabitha, Temwa ndi ena onse timawadalira kunja tikuwadziwa akhale akubwera pa masewero amenewa nde ena azifika mma 15 February ena pa 16." Anatero Haiya.
Iye anatinso komiti yaikulu ya FAM inakambirana kuti Scorchers izisewera mmipikisano yonse yomwe azikhudzidwa poti amangosewera COSAFA yokha.
Timuyi ikasewera masewero apaubale awiri ndi Zambia ngati njira imodzi yosafuna kungokhala poti timu yomwe ankafuna kukumana nayo mu masewero opitira ku WAFCON, Congo, inati siseweranso.
Haiya: Akadzakanika kupita ku AFCON 2027 adzachoka
Mphunzitsi watsopano kutimu ya Flames, Kalisto Pasuwa, wapatsidwa milingo yoti adzatengere Malawi ku mpikisano wa African Cup of Nations mu 2027, adzatengeko COSAFA mu zaka ziwirizi komanso pa masewero opitira ku World Cup omwe atsala asanu ndi imodzi adzapambaneko atatu.
Mtsogoleri wa bungwe la Football Association of Malawi, Fleetwood Haiya, ndi yemwe anatsimikiza za nkhaniyi pa mwambo omuonetsa mphunzitsiyu.
Iye wati mulingo wopita ku AFCON 2027 nde omwe akufunikira kuti akwanilitse afune asafune ndipo ngati sadzatero adzachoka.
"Iyo ya AFCON nde yomwe ayesetse komanso pa zaka zakezi tikufuna COSAFA, mwina chaka choyamba chomanga timu ndipo chinacho atha kudzatero. Komanso masewero aku World Cup tipambaneko atatu." Anatero.
Iye koma wati ngakhale zili momwemo, bungweli lithandize kwambiri Pasuwa kuti akwanitse kuchita bwino pa ntchito yake.
Pasuwa atsogolere timuyi posachedwapa mu mpikisano wa CHAN wa masewero opitira ku mpikisano wa World Cup omwe anayamba kale kusewerako.
Scorchers trip to Zambia on
Football Association of Malawi President, Fleetwood Haiya, says it is the right time their Association stop depending everything on the government but rather find sponsors so that they have all their plans fulfilled.
Haiya said this to confirm Scorchers' trip to Zambia for two friendlies to go as planned after the Malawi National Council of Sports said they will not fund the trip.
He said it is his wish to see Womens Football active and every FIFA window and tournament, the Scorchers will be playing.
"The government doesnt help us only financially but also technically but we need sponsors also as the government can not do it all alone."
FAM secured friendly matches after the withdrawal of Congo Brazzaville in the 2026 WAFCON Qualifiers leading the automatic progress into the second qualifying round.
Pasuwa: It is simple to go to AFCON with cooperation
Newly appointed Flames coach, Kalisto Pasuwa, says it is a very simple job to qualify for the African Cup of Nations but needs to work together in everything and it is possible.
He said this signing a two years deal with the Football Association of Malawi on Wednesday afternoon where he also said he already knows Malawian Football.
"With the local coaches they will join me will be good and i already know Malawian Football, i know the country, players' needs and if we say today we are not playing, i know where to find them." He said.
He has been given a target to qualify for the 2027 African Cup of Nations and he said it is possible if only stakeholders work together in everything.
Pasuwa has qualified for the AFCON once when he guided Zimbabwe National team to the tournament in 2017.
Pasuwa azifika ku matimu onse
Mtsogoleri wa bungwe la Football Association of Malawi, Fleetwood Haiya, wati Kalisto Pasuwa athandizira kukhazikitsa kamenyedwe (philosophy) ya dziko lino pomwe adzifikanso mu matimu achisodzera ndi ya amayinso.
Haiya amayankhula pa mwambo woonetsa mphunzitsiyu kwa anthu atasaina mgwirizano wa zaka ziwiri ndi bungweli.
Iye wati Pasuwa athandizira kupititsa patsogolo mpira wa mdziko muno ndipo ali ndi mphamvu zochuluka zomwe akhale nazo pa ntchito yake.
"Sikuti akhale ku Flames kokha komanso azifika kwa achisodzera paja chaka chino tikukhazikitsa maseweredwe athu nde azionetsetsa ngati zikutheka kumatimuwa angakhalenso ku Scorchers azifika." Anatero Haiya.
Pasuwa akhale mphunzitsi wokhazikika wa timu ya dziko lino mpaka mu 2027 ndipo posachedwapa atsogolera Flames mu CHAN komanso mu masewero opita ku World Cup.
FAM yalonjeza kuthandiza Pasuwa
Bungwe la Football Association of Malawi lalonjeza kuti lipereka thandizo lokwanira kwa mphunzitsi watsopano kutimu ya Flames, Kuti athandize kupititsa patsogolo masewero a mpira.
Mtsogoleri wa bungweli, Fleetwood Haiya, amayankhula pomwe mphunzitsiyu amaonetsedwa kudziko lonse atapatsidwa mgwirizano wa zaka ziwiri.
Iye wati tsopano Pasuwa wapatsidwano mphamvu poti si ogwiriziranso ndipo akuyembekezera zabwino zokhazokha kwa mphunzitsiyu.
"Tsopano ndi nkhani yabwino kuti Pasuwa ali ndi mphamvu. Tiyesetsa kumupatsa sapoti yonse kuti iyeyu achite bwino ndi kutengera mpira wathu patsogolo." Anatero Haiya.
Pasuwa anali mphunzitsi wogwirizira watimuyi ndipo pamasewero omwe anaphunzitsa, Malawi inalepherana 0-0 ndi Burundi komanso kugonjetsa Burkina Faso 3-0.
Haiya: Sitinaphonyeko ndondomeko
Mtsogoleri wa bungwe la Football Association of Malawi, Fleetwood Haiya, wati bungweli linatsata ndondomeko zonse zoyenera kuti alembe Kalisto Pasuwa kukhala mphunzitsi wa Flames.
Iye amayankhula pa mwambo oonetsa mphunzitsiyu kwa anthu a mdziko muno atasaina mgwirizano wa zaka ziwiri ndi bungweli.
Motsutsana ndi bungwe la Malawi National Council of Sports lomwe linadzudzula FAM ati posatsata ndondomeko polemba mphunzitsi, iye anati palibe chinali cholakwika.
"Tinapeza bungwe la aphunzitsi omwe anavomera Pasuwa kenako tinapita ku sub technical committee inavomeranso, kenako komiti yaikulu tinavomeranso nde panalibe cholakwika ndithu." Anatero Haiya.
Pasuwa yemwe kwawo ndiku Zimbabwe wakhala mphunzitsi wogwirizira watimuyi asanatengeretu ntchitoyi ndipo akhale kufikira 2027.
Mamelodi 2_0 sundown
2_0
3_1
Win
Notharm forest