Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
Ernesto, Aida ndi Tiago agawana K20,000 atalosera molondola masewero osachepera 10 sabata yatha pa Owinna.com.
Congrats π
Malawi super league
Players name of Dedza dynamos fc
Bungwe la Super League of Malawi (SULOM) lasuntha masewero a pakati pa FCB Nyasa Big Bullets ndi Civo United kuchoka pa lachinayi, 31 August kufikira lachitatu pa 30 August 2023.
Bungweli silinafotokoza chifukwa chenicheni chosinthira masewerowa koma lati bwalo lomwe adzasewerere likhalabe la Kamuzu.
Komaliza Civo kubwera pa bwalo la Kamuzu, masewero anathera 1-1 ndipo mchigawo choyamba cha ligi, matimuwa analepherananso 1-1 pa bwalo la Civo.
More fire FCB (maule)
Manoma
MPONDA NDI MUNTHALI AKUYAMBA NTCHITO LERO
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya FCB Nyasa Big Bullets wakale, Peter Mponda, ndi goloboyi wa Flames, Brighton Munthali, akuyamba ntchito yawo lero pomwe timu ya Black Leopards ikukumana ndi Pretoria Callies mu masewero oyamba a ligi ya Motsepe Foundation Championship ku South Africa.
Mponda anapita kutimuyi ngati wachiwiri kwa mphunzitsi miyezi iwiri yapitayo ndipo anasankha goloboyi wake wakale ku Sure Stream Academy komanso Wizards FC, Munthali, kuti akagwire nayenso ntchito mdzikoli.
Iwo anakapezako osewera wakale wa Wizards, Raffick Namwera, yemwe agwire nayenso ntchito mu ligi ya chaka chino. Timuyi inatuluka chaka chatha koma inagulanso malo ndipo imenyera nkhondo yoti ilowe mu ligi ya DSTV Premiership. Masewero omwe aliko lero ndi awa:
β’La Masia 15:00 Upington City β’Pretoria Callies 15:00 Black Leopards β’Maritzburg United 19:30 Milford FC
KARONGA YAKONZEKA KUPHA KB
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati timu yake yakonzekera bwino patsogolo pa masewero awo ndi Kamuzu Barracks omwe achitike pa bwalo la Kasungu loweruka.
Kajawa wati timu yake yayenda bwino kuchoka ku Karonga ndipo tsopano maso awo akuyang'ana pa masewero awo ndi KB omwe akufunikira chipambano.
"Akhala masewero ovuta poti KB nayonso ndi timu yabwino koma anyamata akudziwa kufunikira kwa kupambana masewerowa nde pakadali pano anyamata akutsogolo tili nawo abwino kwambiri ndipo zigoli zizipezeka. Anthu abwere ndipo adzaonera mpira wabwino." Anatero Kajawa.
Karonga ikuchokera kogonjetsa timu ya Ekwendeni Hammers 4-1 ndipo ili pa nambala 11 mu ligi ya TNM ndi mapointsi 21 pa masewero 18 yomwe yasewera.
"TIGERS IKUTIPEZA MU NYENGO YOWAWA" - KANANJI
Mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Eliya Kananji, wati timu yake ndiyokonzeka kuti asewere ndi Mighty Wakawaka Tigers ndipo ayesetsa kulimbikira kuti apambane pomwe ali ndi mu nyengo yowawa.
Kananji amayankhula izi patsogolo pa masewero awowa omwe aliko loweruka pa bwalo la Nankhaka ndipo wati zokonzekera zokhudza masewerowa zayenda bwino.
Iye wati padakali pano anyamata onse omwe anali ovulala ali bwino tsopano ndipi zingotengera kuti abwera motani kuchokera kuvulalako. Iye watinso ndi okondwa kamba ka zokambirana zomwe zinalipo mkati mwa sabatayi zomwe zithandize kuchitanso bwino kwa timu.
Eagles ili pa nambala 15 mu ligi ya TNM pomwe yatolera mapointsi 17 pa masewero 18 omwe yasewera.
Arsenal
FOUR BANKERS MISS EXTREME BATTLE
Silver Strikers will not have their four stars namely, Emmanuel Kaunga, Patrick Macheso, Mark Fodya and Chinsisi Maonga as the team look to move up to top of the league if they beat Extreme FC in Friday.
The team's head coach, Pieter de Jongh, has confirmed that Kaunga will have a long term injury while Macheso and Fodya may return in few weeks to come. Meanwhile, the speedy winger Maonga will not be available because he has three yellow cards.
However, De Jongh, has said the team needs to bounce back from a 3-2 loss to Bangwe All Stars last week in style and says his side will be aiming for a win at the Bingu National Stadium.
"Last weekend we were very unlucky against Bangwe All Stars but we have to move on and focus on the next match. We play Extreme FC and i expect a good performance from the team. As professionals we shouldn't let a stumble disturb our run. The players need to enjoy the game. We respect Extreme FC just like any other side so we
Jefrewanoma
ADELEKE WACHIRA KU NOMA
Katswiri wa Mighty Mukuru Wanderers, Adeleke Kolawole, tsopano wachira ndipo atha kuyambapo kuoneka pa bwalo la zamasewero pomwe tsopano wayamba zokonzekera ndi timu yonse.
Katswiriyu anafika mdziko muno mwezi watha atabwereranso pomwe Wanderers inakondabe ntchito zake angakhale kuti anali pa ndandanda wa osewera omwe anachotsedwa chaka chatha.
Iye anabwera atavulala koma tsopano katswiriyu ali bwino ndipo atha kupezeka pa masewero atimuyi ndi MAFCO lamulungu likudzali.
Katswiriyu anabwera ku Wanderers chaka Chatha pomwe anamugula kuchokera ku timu ya Karonga United.
DE JONGH CONGRATULATES BULLETS FOR CAF MATCH VICTORY
Silver Strikers controversial head coach, Peter De Jongh, has congratulated FCB Nyasa Big Bullets after the team secured their away 2-0 win against FC Dragon of Equatorial Guinea in the CAF Champions league last Sunday.
De Jongh spoke this on Thursday in a prematch presser ahead of the team's match against Extreme FC on Friday at the Bingu National Stadium. He said Bullets'win is a good news in the success of Malawi's Football.
"I must congratulate Bullets for the away victory. It's a good job done and I wish them the best in the return leg. A win for Bullets in CAF Champions league is good news for Malawi football and for the country," said de Jongh.
Meanwhile, the De Jongh says his side is ready to face Extreme and he is hoping for the win. Silver Strikers are fourth in the league with 32 points from 18 games and a win will take them top of the table.
SAMBANI RULED OUT FOR THREE WEEKS, 6 WITH FLU AT BULLETS
FCB Nyasa Big Bullets will not have their deputy captain, Precious Sambani, in their second leg of the CAF Champions league match with FC Dragon at the Bingu National Stadium due to a groin injury that has ruled him out for 3 weeks.
The team's head coach, Callisto Pasuwa, confirmed about the news when talking to the team's media ahead of the match. He said Sambani was replaced by Eric Kaonga at half time after seeing that he has been struggling with his leg and after examination, he won't be available for the next three ways.
Meanwhile, Pasuwa said the team's 6 players are under medical monitoring after they came with flu from Equatorial Guinea where they played their first leg match.
"We had 6 players who were down with flu and these re Clyde Senaji, Patrick Mwaungulu, MacFarlane Mgwira, Kesten Simbi, Frank Willard and Ephraim Kondowe who were under medical observation, but they are now improving." Said Pasuwa
"ZA KAMPANI YATSOPANO SINDIKUZIDZIWA" - MPINGANJIRA
Mkulu wa timu ya Mighty Mukuru Wanderers, Roosevelt Mpinganjira, wati zoti ku timuyi kukubwera kampani yoti izithandiza ku ntchito Ina sakuzidziwa.
Mpinganjira wayankhula izi mmawa wa lachinayi pomwe anafunsidwa malingana ndi malipoti omwe masamba ena olemba nkhani analemba lachitatu kuti kampani ina ikubwera kuti izithandiza timuyi.
"Zimenezo sindikudziwa, sindingathe kutsutsa ndithu koma ndati sindikudziwa ine." Anatero Mpinganjira pomwe amayankhula ndi Wayilesi ya Ndirande FM.
Timu ya Wanderers ili ndi makampani angapo monga Mukuru, Ekhaya Foods ndi a Smile life Insurance omwe amathandiza mu ntchito za timuyi.
π¨βοΈ π’πππππππ: Manchester City have announced the signing of Jeremy Doku from Rennes, until the summer of 2028, for around Β£55.5M.
"KUMWEMBE SANAMALIZE KUTIGWIRITSA NTCHITO" - MPINGANJIRA
Mkulu watimu ya timu ya Mighty Mukuru Wanderers, Roosevelt Mpinganjira, wati timu yawo sinathane ndi katswiri wawo Christopher Kumwembe pomwe amukaniza kuti apite kutimuyi ya Green Buffaloes yaku Zambia yomwe inamufuna.
Zinamveka kuti timu ya Buffaloes imafunitsitsa Kumwembe ndipo inalembera Wanderers ndipo timuyi inaika Kumwembe pa mtengo wa $80 million yomwe Buffaloes imafuna mtengowu utsitsidwe koma Manoma amakana.
Mpinganjira wati analandira kalata ndithu yochokera kutimuyi komatu iwo sali okonzeka kugulitsa Kumwembe.
"Kalata tinalandiradi koma tsopano sitinali okonzeka kumugulitsa Kumwembe chifukwa tinamugula kuti atigwirire ntchito ndipo ntchito akadzagwira tidzamulora kuti achoke." Mpinganjira anafotokoza.
Buffaloes inaona Kumwembe kutimu ya Flames pomwe anali ku COSAFA ndipo katswiriyu ali ndi zigoli zokwana zisanu ndi ziwiri mu ligi ya chaka chino.
MALAMULO OMWE MALAWI YASAINA AKHUDZA BULLETS
Timu ya FCB Nyasa Big Bullets ikhonza kuluza omwe amawathandiza a Nyasa Manufacturing company pomwe malamulo a World Health Organization ochepetsa mulingo wa Fodya akukaniza kampani yopanga Fodya kuthandiza masewero a mpira.
Dziko la Malawi lalowa mu mgwirizanowu pa 18 August ndipo yakhala dziko la nambala 183 kutenga malamulowa omwe amachepetsa kapangidwe komanso kasutidwe ka Fodya.
Zina mwa malamulo omwe ali mu mgwirizanowu ndi oletsa kulengezetsa kwa malonda a Fodya mwa njira Ina iliyonse komanso thandizo lopita ku matimu kapena zikho zaku mpira wa miyendo.
Zateremu, Malawi itengera malamulowa ndipo timu ya FCB Nyasa Big Bullets ndi imene ikhudzidwe poti ndi imene imathandizidwa ndi imodzi mwa makampani opanda ndudu. Nyasa yakhala ikuthandiza Bullets kuchokera mu 2015.
Source: Nation
BLUE EAGLES YALONJEZA KUBWERERANSO KWA CHIPAMBANO
Timu ya Blue Eagles yati zokambirana zomwe apanga kutimuyi lachitatu zofuna kukonza kuti timuyi iyambenso kuchita bwino zinali zofunika ndipo timuyi iyambiranso kuchita bwino.
Wapampando watimuyi, Alex Simenti, wati sangakambe zambiri pa zomwe anakambirana pa mkumanowu koma wati mbali zonse zafotokoza mavuto awo ndipo zonse zitha.
"Titaona mavuto aja tinaona kuti ndi kwabwino kuitana mbali zonse zokhudziwa kuti tikambirane ndipo aliyense wakamba mavutowa, mmasewero omwe akubwerawa tiwina ndithu." Simenti anafotokoza.
Mu mkumano womwe unatenga maola asanu ndi likulu la timuyi, unakhudza wachiwiri kwa wamkulu wa apolisi mdziko muno, akuluakulu ena, aphunzitsi, osewera komanso ochemerera kutimuyi omwe amafotokoza nkhawa zawo ndi kuzikonza.
EXTREME IKUYANG'ANA KUCHOKA KUNSI SABATA INO
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Extreme, Elvis Kafoteka, wati timu yawo ndi yokonzeka kwambiri pa masewero awo a mawa ndi timu ya Silver Strikers pomwe wati akuyang'ana zotuluka mu chigwa cha matimu otuluka akapambana masewero awo awiri.
Kafoteka wati akudziwa kuti masewero a Silver Strikers akhala ovuta kwambiri poti Silver ndi timu yaikulu komanso ili ndi osewera odziwa koma wati ayiphunzira timuyi.
"China chilichonse takonza pomwe timaonera makanema a Silver mmasewero awo omwe asewera posachedwa nde tikuyang'ana mu zofooka zawozo. Anyamata omwe atipeza atithandiza kuti tikonze mofooka mwathu chifukwa timapeza mipata yambiri koma timakanika kugoletsa." Iye anatero.
Extreme ili pansi pa ligi ya TNM pomwe yatolera mapointsi 13 pa masewero 18 omwe yasewera mu ligiyi.
IDANA AKHONZA KUBWERERA KU SILVER
Katswiri wa timu ya Flames, Chimwemwe Idana, akhonza kubwereranso kutimu ya Silver Strikers pomwe akulingalira zothetsa mgwirizano wake ndi timu ya Mbeya City.
Izi ndi malingana ndi malipoti a nyuzipepala ya Times yomwe yalemba kuti katswiriyu akufuna kuthetsa mgwirizanowu pomwe akulephera kupeza timu yosewerako mu ma ligi a chaka chino.
Idana ali mdziko la Zambia pomwe amafuna kupita ku imodzi mwa matimu atatu omwe amamufuna koma mpaka pano palibe chachitika. Timu ya Mbeya ikufuna K24 million pa Idana kapena katswiriyu akasewerere timuyi yomwe inatuluka mu ligi yaikulu koma iye akukana.
Ndipo Owinna ili ndi malipoti oti Idana akhonza kupita ku Silver mwaulere akathetsa mgwirizano wake.
Chico
BUNGWE LA NRFA LAPEREKA CHILANGO KWA BWABWA FC
Timu ya mu ligi yaying'ono ya kumpoto ya Bwabwa FC yapatsidwa chilango chosasewera masewero aliwonse a bungwe la Northern Region Football Association atapezeka olakwa pa mlandu omenya oyimbira.
Mu kalata imene bungweli latulutsa lachiwiri, komiti ya bungweli yapeza kuti timuyi inamenya oyimbira pa masewero amu chikho cha Castel Challenge pomwe anakumana ndi Ekwendeni United pa bwalo la Ekwendeni ndipo ochemerera anamenya oyimbira ati amakondera.
Oyimbirawa anapititsidwa ku chipatala komwe anakathandizidwa ndipo bungweli lati mchitidwewu ukhonza kuchotsa moyo wa munthu ndipo wapereka chilangochi kuti aphunzirepo.
Iyi ndi timu yachiwiri kulandira chilango ngati ichi ndi bungweli pomwe Chintheche United inalandira chilango chosasewera kwa zaka ziwiri pa milandu ngati yomweyi. Bwabwa ili ndi maola 48 ngati ikufuna kukasuma posagwirizana ndi chigamulochi.
TIFINYE MAKOLONA POMWE KAMUZU ILI PA NGOZI
Bwalo la Kamuzu ili pa ngozi yoti itha kutsekedwa pomwe bungwe la Football Association of Malawi likuyendera bwaloli kuti lipeze ngati lili lotetezeka kuchititsa masewero a mpira.
Izi zili chomwechi kamba koti bungweli latseka mabwalo awiri a Civo ndi Mzuzu sabata yatha kamba koti sali bwino ndipo akufunika kukonzedwa.
Sabata ino, FAM ikuyendera mabwalo ena mdzikomu ndipo lachiwiri, ayendera bwalo la Kamuzu lomwe mwazina lili kale pangozi chifukwa linaletsedwa kuchititsa masewero ndi matimu akunja ndi bungwe la CAF ndipo FAM inaletsa bwaloli kuchititsa masewero a matimu akuluakulu ngakhale kuti SULOM linanyozera ndikuchititsa masewero a Bullets ndi Wanderers.
Pakadali pano, zotsatira za kuyenderaku zidziwika masabata awiri akudzawa ndipo litha kutsekedwa.
EAGLES YAITANITSA MKUMANO
Timu ya Blue Eagles ikhale ndi mkumano wa akuluakulu a timuyi, osewera komanso aphunzitsi lachitatu pomwe akufuna akawunikire chifukwa chimene timuyi isakuchita bwino.
Izi zikutsatira pempho la mphunzitsi watimuyi, Eliya Kananji, lopita kwa akuluakulu atimuyi kutsatira kugonja 1-0 ndi Moyale Barracks pakhomo pawo sabata yatha.
Mkumano omwe wakonzedwawu ukhudzanso wapampando wakale wa timuyi, Alexander Ngwala, omwe ayitanidwa kuti akamvetse mavuto omwe ali kutimuyi.
Eagles ili pa nambala yachiwiri kuchokera kumunsi ndi mapointsi 17 pa masewero 18 omwe yasewera mu ligi ya chaka chino.
BULLETS IFIKA LERO
Timu ya FCB Nyasa Big Bullets ifika mdziko muno lero pomwe ikuchokera mdziko la Equatorial Guinea komwe yakaphodorako timu ya Dragon FC mu mpikisano wa CAF Champions league.
Mkulu oyendetsa ntchito za timuyi, Albert Chigoga, watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati timuyi ifika masana wa pa bwalo la Chileka mu mzinda wa Blantyre.
Iye watinso matikiti amasewero achibwereza omwe adzachitikire pa bwalo la Bingu lamulungu likudzali ayamba kale kugulitsidwa ndipo wati ali pa mtengo wa K2,000.
Iye wapempha amalawi kuti akasapotere timuyi ndi cholinga choti akagonjetse Dragon poti masewerowa akadali onse ndipo sanathe. Maxwell Gasten Phodo ndi yemwe anagoletsa zigoli ziwiri ku Malabo kuti Bullets ipambane 2-0.
Manchester United have announced that Mason Greenwood will leave the club.
βAll those involved, including Mason, recognise the difficulties with him recommencing his career at Manchester United. It has therefore been mutually agreed that it would be most appropriate for him to do so away from Old Trafford.β
Fixtures
Fixtures added
"PHODO HAS BEEN SCORING BUT OFFSIDE" - PASUWA
FCB Nyasa Big Bullets Head coach, Callisto Pasuwa, says Maxwell Gasten Phodo, has the quality to be used when playing international games saying he is a very good player.
Pasuwa said this after the star netted twice to seal a 0-2 win against FC Dragon in Malabo, Equatorial Guinea and said he has been trusting him that he would perform one day.
"A boy whom I have been trusting, he has been having pressure where people can be saying the boys is not scoring but remember I said these are boys I said when playing against international teams, they can lead attacks when playing with one boy upfront." Said Pasuwa.
He further added that the player had got incredible talent which makes him exceptional and useful for teams upfront and said he has been scoring goals which unfortunately were offside.
Despite an impressive outing in the continental showpiece, Phodo has struggled to score on local scene as he has no goal in the TNM Super league.
"ITS NOT YET DONE" - PASUWA SAYS BULLETS YET TO SAIL THROUGH
FCB Nyasa Big Bullets head coach, Callisto Pasuwa, says there's more to play despite his team claiming a 0-2 win over Dragon FC in Equatorial Guinea after saying their opponents are also equally good.
Pasuwa said this to the team's media after the games and saluted his boys for the wonderful performance in the match.
"Well done to the boys, we did very well starting from the whole set, we looked for the goal and we got it and in most cases we were very solid with how we defended, we just wanted to see if they can build up from the back so we didn't open the spaces. We attacked again and our second goal which I would say was a prize to us." Analyzed Pasuwa.
Meanwhile, despite holding the advantage, Pasuwa said the opponent's are good and there's more work to be done in Malawi.
"It's not a game that I can say we have already progressed, we need to fight at home." Added Pasuwa.
Maxwell Phodo netted both goals in the match.
"TIKUFUNA KUTHERA MU MATIMU ASANU OYAMBA" - MKANDAWIRE
Mphunzitsi watsopano watimu ya Bangwe All Stars, Abel Mkandawire, wati wauza osewera ake kuti akufuna timuyi ithere mu matimu asanu oyambilira mu ligi ya TNM chaka chino ikamadzatha.
Mkandawire amayankhula izi pomwe timuyi inagonjetsa Silver Strikers 3-2 pa bwalo la Kamuzu ndipo iye anati anali okhutira ndi mmene anyamata ake anasewerera.
Iye wati wauza anyamata ake kuti asagone chifukwa akufunitsitsa atamaliza kumtunda kwa ligi.
"Masomphenya anga ndaika kuti tithere mu top 5, ndawauza kale anyamatawa ndipo ndi zotheka." Anatero Abel Mkandawire.
Timuyi ili pa nambala yachisanu ndi chitatu (8) ndipo akuchepekedwa ndi point imodzi kuti afike pa nambala yachisanu mu ligiyi yomwe pali timu ya Kamuzu Barracks.
"I AM A PROFESSIONAL, I NEED WHAT I WANT" - DE JONGH
Silver Strikers head coach, Peter De Jongh, has repeated sayings that it is hard for his team to win the league as he has not been given what he asked the board to do.
De Jongh said this after the game which his side suffered a 3-2 defeat over Bangwe All Stars and said he needed quality players but the board has not given him.
"I need what I want, I am a professional, I wanted quality players but I have not been given so it's hard [to win the league]" said the Dutch.
The Bankers supporters were left furious and wanted to attack their players after the match but security was provided to their players.
The team trail two points to the leaders, FCB Nyasa Big Bullets as they have managed to collect 32 points from 18 games they have played this season on position four.
DE JONGH CLAIMS TO RECEIVE RACISM REMARKS
Silver Strikers head coach, Peter De Jongh, has claimed that he received racism words to the assistant referee in a match that his side lost 3-2 to Bangwe All Stars on Sunday at the Kamuzu Stadium.
De Jongh made the remarks after the match saying its not necessary to be complaining about officiation Everytime but what the linesman spoke to him was bad.
"I cannot everytime complain about the referee and the linesman, that's not important, what is important is what the linesman said to me during the game."
"The linesman from this side said to a very revolt of racism words, I can not repeat it but the linesman said to me bad words." Said De Jongh.
The Dutch has been in a wrangle with referees since the start of the season and has two red cards and four yellow cards since the start of the season. Following the result, Silver remain fourth on the standings with 32 points from 18 games this season.
Photo credit: Aluso Media