Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
Silver Strikers netted four second half goals to beat Santhe ADMARC 4-0 in a friendly thanks to goals from Paul Kamsungwi, Uchizi Vunga, Binwell Katinji and Emmanuel Muyira.
The Bankers will face Civo United in a Lilongwe derby on Sunday.
FIRST CAPITAL CITY DERBY IS HERE!
The capital city derby of 2024 will be played on Sunday as Silver Strikers play Civo United at the Champions Stadium in a Pre-Season friendly.
Fans will have to pay K3,000 at the open stand to watch the mouthwatering match
The big thing to witness is how two strikers, Binwell Katinji and China Chirwa, will perform against their former sides.
"MASEWEROWA AKUTIPATSA CHITHUNZITHUNZI CHABWINO" - MPONDA
Mphunzitsi watimu ya Silver Strikers, Peter Mponda wati masewero omwe akusewera akupereka chithunzithunzi chabwino pa mphamvu za osewera omwe atagwilitse ntchito chaka chino.
Mponda amayankhula atatha masewero omwe agonjetsa Bangwe All Stars 3-0 pa bwalo la Aubrey Dimba ku Mchinji ndipo wayamikira osewera poti akutsatira zomwe akuwauza.
"Masewero akupatsa mwayi oti tidziwe kuti ndi osewera ati omwe atha kusewera mphindi 90 komanso ena oti atha kusintha zinthu titavutika. Masewero alero timavutika mchigawo choyamba, mmene tinakonzera simmene zinalili komabe titasintha komanso kuwayankhula nthawi yopumulira, osewera anachita bwino kwabasi." Anatero Mponda.
Mmasewerowa, Binwell Katinji, Gift Chunga komanso Chinsisi Maonga ndi omwe anagoletsa zigoli za timuyi. Iwo asewera masewero atatu ndi MAFCO komanso Kamuzu Barracks kupatikizira a Bangwe ndipo apambana onse.
@clementina tatumiza
SILVER SIGN KAMSUNGWI
Silver Strikers has announced the signing of former FCB Nyasa Big Bullets midfielder, Paul Kamsungwi, the club has confirmed.
Kamsungwi joins the Bankers on a two year deal after returning from professional football in Mozambique.
Meanwhile, the Bankers has also promoted Innocent Mtonga and Eustice Mwale from the Reserve side and have each one signed three year deals.
Komiti ya ochemelela yomwe imayang'anila za umoyo wa osewela kutimu ya Silver Strikers, yathandiza osewela otchedwa Tatenda M'balaka yemwe pakadali pano ndiovulala.
Mwambo opeleka ndalamazi unachitika dzulo pabwalo la Silver pakutha pamasewelo omwe ma Banker anagonjetsa MAFCO FC 3-2.
Poyankhula atatha kupeleka thandizoli, King 'No Fear' Malaya yemwe ndi wapampando wa ochemelela komaso membala wa komitiyi, anati apeleka ndalama yomwe sanatchule kuchuluka kwake, kuti ithandize pazosowa zina za osewelayu komaso ngati chilimbikitso kwa osewela.
Iye anapitiliza kulimbikitsa ochemelela a timuyi kuti apitilize kulimbikitsa osewela a Silver Strikers ndimathandizo osiyanasiyana akakhala ovulala.
Ndalamazi zinasonkhedwa pa gulu la WhatsApp la komitiyi yomwe inasonkhetsanso masapota ena omwe anafika pa bwalo la Silver dzulo.
WOLEMBA: Erik Chiputula
SILVER ICHOTSA OSEWERA KHUMI
Timu ya Silver Strikers ikuyembekezeka kuchotsa osewera okwana khumi pomwe ikuyamba zokonzekera zokhwima za ligi ya chaka chino.
Mkulu wa timuyi, Patrick Chimimba, watsimikiza za nkhaniyi ndipo wati timuyi ikufuna ntchito za osewera omwe asewera mu timuyi kuti izichita bwino komanso kuti amadikira lipoti ya aphunzitsi atimuyi.
Osewera monga George Chaomba, Tathedwa Willard, China Chirwa ndi ena ndi omwe akumveka kuti atha kuona nsana wanjira.
MPONDA INCLUDE ZICCO MKANDA IN SILVER'S PANEL
Silver Strikers head coach has announce the inclusion of his former Striker at FCB Nyasa Big Bullets, Zicco Mkanda, to be the team's strikers in the coming 2024 season.
Mjojo said this on Friday as he unceiled his backroom staff for the coming season and believes Mkanda will help him a lot.
"The reason for bringing Mkanda, he has been one of the finest strikers in this years and with his experience he will help the youngsters, I think the players also have seen him playing so they will learn from him." Said Mponda.
Here is how the whole technical panel appears:
Head coach: Peter Mponda First deputy: Peter Mgangira Second deputy: Young Chimodzi Jr Strikers trainer: Zicco Mkanda Goalkeepers trainer: Victor Mphande Team manager: Emmanuel Chipatala Welfare manager: Cassim Wasiri Team doctor: Chikondi Kaminga Physiotherapist: Andrew Ntalimanja Data analyst: Taonga Chimodzi
Reported by Hastings Wadza Kasonga Jr
"SILVER INALI TIMU YAKUMALOTO KWANGA" - CHIKOOKA
Goloboyi yemwe timu ya Silver Strikers yangosaina kumene, George Chikooka, wati linali khumbo lake kudzasewerako timu ngati Silver Strikers ndikuti agwira ntchito molimbikira.
Iye amayankhula atasaina mgwirizano wake wa zaka zitatu ndi timuyi kutsatira kuchoka kutimu ya Chitipa ndipo wati palibenso chilendo chilichonse chomwe ataone ku Silver Strikers.
"Ndine wokondwa pobwera kutimuyi, anali maloto anga ntadzasewerako kutimuyi ndipo ndingoyamika Mulungu pokwanilitsa malotowa. Palibenso chilendo chilichonse chomwe ndingaone, enawa takhala tikusewera nawo nde palibe chilendo." Anatero Chikooka.
Katswiriyu anali mmodzi mwa magoloboyi omwe anachita bwino mu ligi ya chaka chatha pomwe sanagoletsetse mmasewero 12 ndipo alimbirana pa malo oyamba pagolo ndi Charles Thom komanso Pilirani Mapira.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
"MASAPOTA AYEMEKEZERE ZAMBIRI ZOKOMA" - KATINJI
Katswiri yemwe wasainidwa nditimu ya Silver Strikers, Binwell Katinji, wati ochemerera atimuyi ayembekezere zabwino zokhazokha pomwe wati agwira ntchito ngatinso mmene amachitira kumatimu ena.
Iye amayankhula atasaina mgwirizano wa zaka ziwiri kutimuyi kutsimikiza za kubwereranso kutimuyi ndipo wati ndi wokondwa kubwereranso kwawo.
"Ndine wosangalala poti ndabwereranso ku Silver, nditimu yoti ndasewerapo, khalidwe lake ndikulizidziwa komanso zambiri nde ndasangalala. Masapota amayembekezera zambiri koma ndi zoti sindingagwire ntchito ndekha komabe ayembekezere zabwino zambiri ngati mmene ndimachitira ku matimu ena." Anatero Katinji.
Katswiriyu wapita kutimuyi mwaulere kutsatira kutha kwa mgwirizano wake ndi Civo komwe anamwetsa zigoli 12 mu ligi ya chaka chatha.
Timu ya Silver Strikers ikupitilira kuchita zododometsa pomwe akukonzekera ligi ya chaka cha 2024 pomwe agula bus ya Marcopolo.
Ma Banker akhala achiwiri mu 2024 kuonetsa galimoto yamtunduwu pomwenso galimoto ya Creck Sporting Club idzaonekanso chomwechi.
"SINDINAGANIZE KAWIRI ATANDIPEZA A SILVER" - CHIPALA
Wosewera pakati ndi kutsogolo yemwe timu ya Silver Strikers yasaina lachiwiri, Charles Chipala, wati linali khumbo lake lalikulu kuti adzasewereko timu yaikulu ngati Silver Strikers.
Iye amayankhula pomwe amamuonetsa kutimuyi kuti wasaina mgwirizano wa zaka zitatu pomwe tsopano wachoka kutimu ya Dedza Dynamos pa ndalama zomwe samaziulule.
Iye wati ndi wokondwa kupita kutimuyi ndipo akuyembekezera kuti ayithandiza timuyi kuchita bwino ndipo iye athandizika kuti apite patsogolo ndi mpira wake.
"Kubwera Ku Silver Strikers ndi chinthu chapamwamba kwambiri chifukwa ndi zimene ndakhala ndikukhumbira nthawi yaitali nde atandipeza sindinaganizirenso kawiri koma kuvomera." Anatero Chipala.
Iye wakhala osewera wachitatu kupita kutimuyi patsogolo pa ligi ya 2024 pomwe inatenga Christopher Gototo komanso Macdonald Lameck kuchokera ku Dedza Dynamos.
"NDITHOKOZE MULUNGU NDABWERA KUTIMU YAIKULU" - LAMECK
Katswiri yemwe wangosaina mgwirizano ndi timu ya Silver Strikers, Macdonald Lameck, wati akhala osewera olimbikira kwambiri chifukwa ochemerera atimu yaikulu amafuna zipambano zokhazokha basi.
Iye amayankhula pomwe amatikitira mgwirizano wa zaka zitatu kumalizitsa za kuchoka kwake kutimu ya Blue Eagles. Iye wati Blue Eagles inamusamalira kwambiri ndipo zinamutsegulira mwayi wochita bwino.
"Ndithokoze Mulungu pondipatsa mwayi woti ndisewere timu yaikulu ngati Silver ndipo ndikukhulupilira kuti ndichita bwino kwambiri.Kusewera timu yaikulu ngati Silver chimafunikira kwa masapota ndi chimodzi basi, kupambana." Anatero Lameck.
Katswiriyu anachokera ku FCB Nyasa Big Bullets kuti apiteko ku Blue Eagles komwe wasewera zaka ziwiri ndipo mu nthawiyi watumikirakonso timu ya Flames.
DE JONGH WACHOKA KU SILVER
Mphunzitsi wa Silver Strikers, Peter De Jongh, wasiya ntchito yake kutimuyi pomwe akufuna akaone zina ku matimu ena.
Malingana ndi malipoti, mphunzitsiyu wauza akuluakulu atimuyi kuti athetse mgwirizano wawo kamba koti sali wokondwanso kukhala kutimuyi.
Uyu ndi mzungu wachiwiri kutsanzika kutimu kwake pomwe mphunzitsi wakale wa Mighty Mukuru Wanderers, Mark Harrison anatsanzika mwezi watha.
DE JONGH RETURNS AND TO START PREPS JANUARY END
Silver Strikers head coach, Peter De Jongh, will cut his holiday short as he is expected to return to Malawi on 28 January 2023 to start preparations for the 2024 season a day later.
De Jongh said this in an interview that he has submitted his plans to the team's board already and that the team will now give him what he has asked pointing out that the issue of Chimwemwe Idana cost him last year.
“I have also indicated the challenges we faced such as the absence of [Chimwemwe] Idana in seven games, our preparations being distracted by the national team engagements as well as the failure to sign the players I recommended. So, I believe all these aspects will be taken into consideration." Said De Jongh.
He further said he rejected a job in Morocco because he loves Silver Strikers, its players and Malawi as a country. Meanwhile, the team's board is assessing him and they are rumoured to be linked to Peter Mponda to replace him.
DEAL DONE
Silver Strikers has completed the signing of Macdonald Lameck from Blue Eagles on a two year contract.
He becomes the second signing for the Bankers after roping in Christopher Gototo from the Eagles.
"CHANZERU NDI KUWINA OSATI KUMENYA BWINO" - M'GANGIRA
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Silver Strikers, Peter M'gangira, wati ndi zabwino kuti timu yake yapitilira mu mpikisano wa Castel Challenge Cup ndipo zoti sanamenye bwino sizofunikira kwambiri.
Iye amayankhula atatha masewero omwe apambana 4-2 pa bwalo la Bingu lachitatu ndipo wati timu yake inachilimika angakhale kuti simasewera bwino mmasewerowa.
"Tinayamba movutika kwambiri ndipo anzathuwa anatichinya komabe anyamata anayesetsa mpaka tinatsogola kenako kachibwana tinapangitsa penate koma mphunzitsi kopumulira anawayankhula osewera ndipo agwiradi ntchito." Anatero M'gangira.
Iye wati timu yake ichita chothekera kuti mipikisano iwiri ya Airtel Top 8 komanso Castel yomwe ali mu ndime ya matimu anayi atengeko mwina chimodzi kapena zonse. Zateremu, timuyi ikumana ndi Bangwe All Stars mu ndime ya matimu anayi.
"KAJOKE WAS COMING BUT WENT BACK TO BULLETS" - DE JONGH EXPLAINS HOW HE MISSED THE LEAGUE
Silver Strikers head coach, Peter De Jongh, says what he will do next year in order to win the TNM Super League with the team will be discussed with the board and not the media.
The Dutch said this after his team failed to snatch the league out of FCB Nyasa Big Bullets' hands as the teams drew 1-1 at the Kamuzu Stadium and he explained what led to lose the league to Bullets.
"I asked for a striker of which I saw at training that they do not have a striker, he was not coming then Kajoke was coming, you know the story, he went back to Bullets and scoring many goals for them. The same with Idana, we did not have him in some games in the league but Idana is a very good player plus the COSAFA Cup made some players to leave the team for a non-FIFA Calendar tournament." Said De Jongh.
In the game against Bullets, De Jongh was shown a red card yet again for unsporting behaviours. The Bankers have fini
"TIMAONA NGATI SIZITHEKA KOMA ZATHEKA" - M'GANGIRA
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Silver Strikers, Peter M'gangira, wathokoza anyamata ake kamba kochilimika mpaka kupambana pomwe wati amaona ngati nzovuta kuti angatero.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe Chimwemwe Idana anagoletsa pa mphindi 95 kuti Silver Strikers igonjetse Kamuzu Barracks 2-1 mu ligi ndipo wayamikira anyamata ake.
"Analidi masewero ovuta koma tinasewera bwino makamaka mchigawo choyamba pomwe tinatsogola pa chilichonse koma kachibwana mchigawo chachiwiri kanatibweretsa mmbuyo komabe pomwe zimaoneka ngati sizitheka, zatheka." Anatero M'gangira.
Timu ya Silver Strikers yafika pa nambala yachiwiri mu ligi ndi mapointsi 56 kutsatira chipambanochi ndipo izipempherera kuti Karonga United igonjetse FCB Nyasa Big Bullets kuti iwo idzagonjetse Bullets yokha mmasewero omaliza.
DE JONGH STILL HOPES TO WIN THE LEAGUE
Silver Strikers head coach, Pieter De Jongh, has said that his team still has hopes of winning the 2023 TNM Super League and that they will fight till the end.
The Dutch said this on Friday ahead of the team's match with Ekwendeni Hammers on Saturday which he says it will be tough but a win is a must for the Area 47 side.
"We play on Saturday at home against Ekwendeni Hammers and this is not just an ordinary game for us as we aim for a win. As usual we respect our opponents, they will come for a win as well as they want to fight relegation. So currently we haven't given up on our hope for winning the title. With the remaining games we hope to finish at 59 points," he said.
He further said he would love to play the match on Sunday to give a rest to the players but nothing can happen and they will play Hammers. After dating Ekwendeni, the Bankers will have to play Kamuzu Barracks and FCB Nyasa Big Bullets to wind up the league.
Reported by Has
"OSEWERA ATOPA KOMA SITINGACHITIRE MWINA" - M'GANGIRA
Wachiwiri kwa mphunzitsi watimu ya Silver Strikers, Peter M'gangira, wati timu yawonso ikhonza kukhala ndi madando oti osewera atopa koma poti palibe chomwe chingasinthe iwo amalizitsabe kusewera.
Iye amayankhula izi patsogolo pa masewero awo ndi timu ya Ekwendeni Hammers pa bwalo la Bingu loweruka ndipo wati timu yake yakonzeka kwambiri.
Iye wati osewera onse apezeka pomwe omwe anali ovulala achira ndipo pa nkhani ya kutopa, iye wati adziwa mongowagwiritsa ntchito mwake.
"Ndi nkhani yoti atopadi koma poti kuno ndi ku Malawi, kudandaula palibe chomwe chingasinthe nde nkhani ndi kungodziwa kuwagwiritsa osewerawa kuti onse asamatope." Anatero M'gangira.
Timu ya Silver inapambana 3-1 mu chigawo choyamba pa bwalo la Mzuzu ndipo ikupita mmasewerowa ili pa nambala yachitatu ndi mapointsi 50 pamasewero 27 omwe yasewera.