Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
NYONI ALI KU FOMO
Wachiwiri kwa mphunzitsi wakale wa Ekwendeni Hammers, Luckson Mauluka Nyoni, tsopano ali ku Mulanje pomwe aphunzitse nawo timu ya FOMO.
Nyoni akhala wachiwiri kwa mphunzitsi watimuyi, Gilbert Chirwa, mu chaka choyambilira cha mu TNM Supa ligi cha timuyi.
Awiriwa anagwirapo limodzi ntchito ku Ekwendeni Hammers mu 2022 pomwe timuyi inachita bwino koopsa Chirwa asanapite ku Dedza Dynamos.
FOMO YASANKHA BWALO LA MULANJE PARK
Timu imene yangolowa kumene mu Supa ligi, FOMO, yasankha bwalo la Mulanje Park ku bungwe la Football Association of Malawi kuti ndi limene agwiritse ntchito ngati bwalo lawo lapakhomo patsogolo pa ligiyi.
Timuyi yasankha bwaloli poti iyo ndi yaku Mulanje ndipo apereka ku FAM ngati mbali imodzi yokwanilitsa zomwe timu ikuyenera kukhala nazo pa ndondomeko ya Club licensing.
Ndipo woona za ndondomekoyi, a Cassper Jangale, atsimikiza kuti tsopano ayamba kuyendera mabwalo osiyanasiyana mdziko muno kuyambira 26 February ndipo ndandanda wa mabwalo omwe avomerezedwe udzatuluka pa 13 March.
Nayo khonsolo ya mzinda wa Mulanje yati ikukonza zofunikira pa bwaloli kuti likhale pa mulingo wochititsa masewero amu ligi yaikuluyi.
Timuyi imalephera kugwiritsa ntchito bwaloli ikusewera mu ligi yaing'ono kamba ka kusamvana pakati pa iwo ndi khonsoloyi ndipo amakasewera ku bwalo la Esperanza mu mzindawu.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
"NDAWAUZA KUTI ATIPEZERE ENA" - CHIRWA
Mphunzitsi yemwe walembedwa kumene kumbali ya timu ya FOMO, Gilbert Chirwa, walonjeza timuyi kuti ichita bwino kwambiri mu chikho cha Supa ligi ndipo wawauza eni ake kuti amupezere osewera atsopano.
Iye amayankhula pomwe amalandilidwa kutimuyi atasaina mgwirizano wa chaka chimodzi nditimuyi yomwe yangolowa kumene kuchokera mu ligi yachigawo chakummwera yomwe anapambana atagonjetsa Ntopwa.
Chirwa, yemwe chaka chatha amaphunzitsa ku Dedza Dynamos, wati wapempha mkulu watimuyi kuti ayesetse kumupezera osewera ena atsopano kuti alimbitse timuyi.
"Pa zokambirana zathu ndinawapempha kuti mwina atipezere osewera ena atsopano kuti alumikizane ndi ena omwe alowetsa timuyi mu Supa ligi, ndikukhulupilira kuti choncho zithandiza kuti timu izichita bwino." Iye anatero.
Iye anatinso kutimu iliyonse yomwe amapita amachita bwino ndipo akuyembekezera kuti ku FOMO zichitanso chimodzimodzi ndipo ikamatha chakachi idzakhala yatsala mu ligiyi. Kumbali ya omuthand
"I WILL ALSO HELP ANOTHER TEAM TO BE PROMOTED" - MSUKWA
FOMO FC head coach, Mapopa Msukwa, has advised the team coach that will cone at the team to beef up the team's squad in few areas in order to perform well in their debut season in the TNM Super League in 2024.
Msukwa said this after guiding the team into the Top flight league thanks to a 4-3 win in penalty shootouts against Ntopwa on Sunday at the Kamuzu Stadium but said he has left the at least in good condition.
"Unfortunately, I will not be with the team in the league because I have CAF C so they will look out for another coach with CAF B or A. The other coach will have to beef up the team but I have left them on a good place, I will maybe go and help another team earn promotion into the Super League again." Said Msukwa.
This will be the first ever time for the Mulanje Based boys to play in the top flight league and they have almost two months to prepare for the 2024 season.
Reported by Hastings Wadza Kasonga Jr
"OYIMBIRA NDI YEMWE WATIPWETEKA" - SOSTEN
Wapampando wa timu ya FOMO FC, Hadweck Sosten, wati timu yake yagonja chifukwa choti oyimbira, Mayamiko Kanjere, amakondera timu ya FCB Nyasa Big Bullets Reserve mmasewerowa.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe agonja 2-1 pa bwalo la Kamuzu ndipo wati Kanjere akumudziwa kale kuti sayimbira bwino.
"Anali masewero abwino, tamenya bwino kwambiri muone timasunga mpira kwambiri kuposa iwowa timawamenya koma oyimbira ziganizo zake sizinali bwino. Anawapatsa penate yabodza pomwe iwo akagwira samayimba nde iyeyu watipweteka." Anatero Sosten.
Iye watinso timuyi ilowa mu Supa ligi ya chaka cha mawa. Kutsatira kugonjaku, timu ya FOMO ikadali pa nambala yachiwiri mu gulu B ndi mapointsi 33 pa masewero 18.
Fomo win case, to face Nyasa Big Bullets Reserve By Grecium Gama:
Mulanje-based side, Fomo, will face Nyasa Big Bullets Reserve in the semifinal of the Thumbs Up Southern Region Football... times.mw