"BWENZI TIKUTI BLUE EAGLES YAPEZA 3 POINTS" - KANANJI
Mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Eliya Kananji, wati timu yake inasewera mwapamwamba moti ikanatha kupambana mmasewero omwe yalepherana ndi FCB Nyasa Big Bullets koma mipata yomwe anayipeza aphonya.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe alepherana 0-0 pa bwalo la Nankhaka ndipo wati zolakwika zonse akonza kuti mmasewero awo ndi MAFCO adzapambane.
"Tiyamike Mulungu kuti takumana ndi anzathu a Nyasa Big Bullets, tithokozenso anyamata athu asewera bwino kwambiri mwina zangochitika koma bwenzi tikuti Blue Eagles yatenga 3 points koma tikonza molakwika kuti ndi MAFCO tidzapambane." Anatero Kananji.
Kutsatira zotsatirazi, Blue Eagles yasuntha mu ligi ya TNM pomwe tsopano yafika pa nambala yachisanu ndi chitatu (8) ndi mapointsi 35 pa masewero 29 mu ligiyi.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores