"NDIWINA UTSOGOLERI WA FAM" - VINGULA
Mmodzi mwa anthu omwe aonetsa chidwi choimira pa mpando wa utsogoleri wa bungwe la Football Association of Malawi, Balawala Vingula, wati anthu asadere nkhawa poti apambana zisankhozi.
Iye amayankhula izi pa wayilesi ya Angaliba FM madzulo a lachiwiri ndipo wati pofika pa 14 November, dzina lake likhala litamveka kuti wasankhidwa kuti akayime nawo pa chisankhochi.
"Nomination atseka pa 15 November koma ikamadzati 14 mudzamva kuti dzina langa alipanga nominate ndipo pa zisankhozi ndikukawinanso ndi ine." Anatero Vingula.
Padakali pano, mtsogoleri wa bungweli, Walter Nyamilandu Manda komanso mtsogoleri wa Bungwe la Super League of Malawi, Fleetwood Haiya ndi omwe alandira kale ma nomination.
Reported by Hastings Wadza Kasonga Jr
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores