DE JONGH AKUBWERA LACHINAYI
Mphunzitsi wa timu ya Silver Strikers, Pieter De Jongh, afika mdziko muno lachinayi likudzali pomwe tsopano mapepala ake atheka kuti apitilize ntchito yake.
Mneneri watimuyi, Willard Chakanika, watsimikiza kuti timuyi yapangitsa chitupa cha zaka ziwiri tsopano pomwe Silver yalipira K2 million imene inkafunikira kugwirira ntchitoyi.
Mphunzitsiyu ali mdziko la Kenya komwe kuli banja lake komwe anapita pa 22 September 2023 kamba koti chitupa chake chakale chinatha mphamvu.
Mu nthawi imene iye kunalibeko, Silver yakwanitsa kugonjetsa Mighty Mukuru Wanderers komanso Civo United mu Airtel Top 8 ndi Supa ligi iliyonse.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores