"SIKUTI ZAYERA KOMA TICHILIMIKABE" - KANANJI
Mphunzitsi watimu ya Blue Eagles, Eliya Kananji, wati timu yake sinapezebe mtendere ndipo akuyenera kuchilimika angakhale atalikirana ndi nambala za matimu otuluka mu ligi.
Kananji amayankhula izi atatha masewero omwe apambana 2-1 ndi timu ya Ekwendeni Hammers pa bwalo la Nankhaka ndipo wati anawapempha osewera ake kuti apambane chifukwa Ekwendeni imawavuta kwambiri.
Iye wati anyamata ake akumvera zimene akuuzidwa koma wati asatayilire chifukwa mtendere sunawachokere.
"Yakhala ili nyimbo kuti tikuyenera kuchoka kumunsi tili kuja nde padakali pano ligi yavuta nde anyamata sakuyenera kugona komabe tikuyesetsa kuti tichokeretu." Anatero Kananji.
Timu ya Blue Eagles yafika pa nambala 10 mu ligiyi pomwe tsopano ili ndi mapointsi 27 pa masewero 22 amu ligiyi.
#Tawonga2023
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores