BANDA WAYAMIKIRA OSEWERA ACHISODZERA KU FLAMES
Mtsogoleri wa osewera kutimu ya Flames, John Banda, wayamikira osewera omwe ndi achisodzera kutimuyi kamba kochita bwino ndi timuyi ku mpikisano wa COSAFA komwe anathera pa nambala yachinayi.
Banda amayankhula izi patsogolo pa masewero awo ndi timu ya Guinea yomwe iye walonjeza kuti iwo apanga kuthekera kulikonse kuti apambane.
Iye wati osewera achisodzera akuchita bwino kwambiri kutimuyi ndipo ngati angagwirane manja ndi achiyambakale akutimuyi, timuyi ipambana masewerowa.
Malawi ikukumana ndi Guinea mu masewero opitira ku mpikisano wa African Cup of Nations koma matimu omwe anadutsa kale ndi Egypt komanso Guinea yomweyi.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores