"TIKUYENERA KUPAMBANA MASEWEROWA" - SIBALE
Mphunzitsi wachiwiri kutimu ya Blue Eagles, Christopher Sibale, wati timu yake ikuyenera kupambana masewero awo ndi timu ya Karonga United ndi cholinga choti achoke kumunsi kwa ligi komwe iwo ali.
Iye amayankhula izi patsogolo pa masewero omwe aliko pa bwalo la Karonga lamulungu ndipo wati akudziwa kuti akhale ovuta chifukwa choti Karonga ikuchita bwino.
"Akhala masewero ovuta poti Karonga ikuchita bwino komabe ife takhonzeka kuti tikachite bwino, anyamata tawauza kuti akapita kutsogolo azigwiritsa ntchito mwayi uliwonse omwe aziupeza." Anatero Sibale.
Iye wati chipambano mtsiku la lero chikhale chabwino kwambiri poti timuyi ichoka kumunsi komwe iwo ali ndikuti asadzatuluke mu ligi ya TNM.
Eagles ili pa nambala yachitatu kuchokera kumunsi pomwe ali ndi mapointsi 20 pa masewero 19 omwe asewera mu ligi ya chaka chino.
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores