DE JONGH ALANDIRA CHILANGO
Bungwe la Super league of Malawi, ikudikira malipoti kuti iunike khalidwe lomwe mphunzitsi watimu ya Silver Strikers, Peter De Jongh anaonetsa pomwe timuyi inafanana mphamvu 0-0 ndi Chitipa United pa bwalo la Civo.
Mlembi wa bungwe la SULOM, Williams Banda wati izi ndi zochititsa manyazi ndipo khalidwe lake siloyenera kuonetsa iyeyu monga mphunzitsi.
Banda wati bungwe lawo lidikira malipoti ammasewerowa ndipo De Jongh akhonza kulandila chilango. Mmasewerowa, ochemerera wina wa Silver anakathira mkodzo pa golo la Chitipa ndipo bungweli liunikanso pa milandu.
De Jongh wakhala asakuonetsa khalidwe labwino chipitireni ku Silver Strikers ndipo anthu osiyanasiyana adzudzula mchitidwe wakewu
Khalidwe alibe mkumluyu
Login with Facebook to post predictions, updates & live scores