Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
"TSOPANO TIYAMBA KUWINA" - MUYOMBE
Mphunzitsi watimu ya Baka City, Davie Muyombe, wati tsopano timu yake ikuphunzira pang'onong'ono ligi ya TNM ndipo mmasewero otsatira ikhale ikupeza chipambano chawo choyamba.
Iye amayankhula atatha masewero omwe afanana mphamvu 0-0 ndi MAFCO ndipo wati mipata yomwe anaphonya mchigawo choyamba ndi yomwe akanatha kupambanira.
"Tinasewera bwino koma taphonya mmipata ya mchigawo choyamba mwina tikanatha kutsogola 2-0 koma mchigawo chachiwiri sitinali bwino timamenya mpira wa mmwamba komabe tikuphunzira apa tapeza point imodzi ndekuti masewero otsatira tipeza chipambano poti Ife tikuchokera ku Simama nde tikuphunzira ndithu." Anatero Muyombe.
Timu ya Baka City tsopano yapeza point yawo yoyamba mu ligiyi pomwe tsopano yasuntha kufika pa nambala 13 ndi point imodzi pa masewero atatu.
"BAKA CITY ILI NDI TSOGOLO LABWINO" - MUYOMBE
Mphunzitsi watimu ya Baka City, Davie Muyombe, wati timu yake ikhale ikuchita bwino muligi ya TNM mmasewero akutsogoloku kamba koti akadaphunzira mmene mpira wamu ligiyi umayendera.
Iye amayankhula atagonja 2-1 ndi timu ya Mzuzu City Hammers kuti akhale masewero awiri opanda chipambano ndipo wati timu yake ndi yabwinobwino komanso ili ndi tsogolo labwino.
"Palibe mavuto aliwonse timu ilibwinobwino kungoti mwina poti tikumenya ligi yaikulu koma tiphunzira mmene mpira wake umayendera nde tikasewera masewero asanu kapena kudutsa apo tidzachita bwino kwambiri." Anatero Muyombe.
Iye anatinso masewerowa akanakhala ophweka kuti apambane koma ziganizo zina za oyimbira sizinali zabwino mmasewerowa.
Timuyi ili pa nambala 15 pomwe ilibe point iliyonse pa masewero awiri amene Iwo asewera.
"IT'S A MUST WIN AGAINST HAMMERS" - MUYOMBE
Baka City interim coach, Davie Muyombe, said he is targeting a win as they play Mzuzu City Hammers on Saturday at the Mzuzu Stadium so that it brings the confidence of players in the season.
Muyombe said this on Friday ahead of the match and said the departure of Oscar Kaunda has seen some things sorted at the club and is looking to perform well this season.
"We are well prepared for the match, our training had been good and the boys are in good shape, no injuries and we are out to win. A win will help to bring molare to the team so that we start winning games so we are ready." Said Muyombe.
He further confirmed that the players that missed their league opener last weekend have been cleared and will play against Hammers.
The rookies suffered a 0-1 defeat against Karonga United in a Kyungu derby last week and they are the only rookie not to have a win this season.
"WE MISSED SOME OF OUR PLAYERS" - MUYOMBE
Baka City started their journey in their debut Season on a low note after suffering a 1-0 loss in a Kyungu Derby against Karonga United on Sunday afternoon.
Substitute, Blessings Mwalilino scored the lone goal to seal the win for Karonga but Assistant coach for Baka City, Davie Muyombe, said he miss some players who are yet to be cleared by their teams.
"We played very well and everything is quite okay only that we were slow in defense but attacking well so we will try to fix that. We have some players who did not play because we are still discussing with their teams so when they come I think the journey in the league will be easy." Said Muyombe.
He also said he faces two experienced coached and has made him learn more from the match. The team is on 11th with no point from their first game.
NEWS
Baka City head coach, Oscar Kaunda, has resigned from his position at the team despite having few days to kick off the 2024 season.
It has been heard that Kaunda and the team have not agreed on some terms such as salary and has opted to resign.
He was employed by the team two months ago to lead them in their debut season.
"I PROMISE GOOD RESULTS TO THE TEAM" - KAUNDA
Newly appointed Baka City coach, Oscar Kaunda, said he will work hard to bring good results to the team so that they stay in the league for years.
Kaunda said this on Monday when the club confirmed him as the new head coach and said he hopes to work well with his backroom staff for the betterment of the team.
"I am very happy to join the Baka family, they have trusted to deliver and its not only for me but with my fellow coaches will work together so that we perform well and stay in the team. I promise nothing but good results in our games." Said Kaunda.
Kaunda has not been with a team since his departure at Civo United and coached teams such as Karonga United and Mighty Mukuru Wanderers in the past years.
The Clever boys were promoted into the top flight league after winning the SIMSO and Innobuild Northern Region Football League in 2023.
Reported by Hastings Wadza Kasonga Jr
BAKA YATENGA KAUNDA NGATI MPHUNZITSI
Mphunzitsi wakale watimu ya Civo United komanso Mighty Mukuru Wanderers, Oscar Kaunda, wasankhidwa kukhala mphunzitsi watimu ya Baka City mu chaka cha 2024.
Timuyi yalengeza za kubwera kwa Kaunda lolemba pomwe akuyamba zokonzekera za ulendo wawo mu ligi ya chaka chino.
Kaunda athandizidwa ndi Davie Muyombe ngati wachiwiri wake yemwe ndi amene analowetsa timuyi mu ligi ya TNM.
BAKA CITY RULES KARONGA
SIMSO and Innobuild Northern Region Football League champions, Baka City, continue to humble giants after beating Karonga United 1-0 in a friendly organized by Willy Yabwanya Phiri at the Karonga United on Wednesday afternoon.
Substitute, Lupakisho Kazingo, needed only 11 minutes to head home two minutes from time to grant the Clever boys a sweet victory in a newly formed Karonga derby.
After a barren 45 minutes, Baka went close through Mwakyembe and Sherrif Shamama whereas Davie Tobias hit the post for Karonga before Kazingo's introduction on 77th minute to seal the win on 88th minute.
In other games, Karonga United Reserve lost 1-0 to Karonga United whereas Karonga United Women beat St Marys Women 3-1 on the same pitch.
BAKA CITY YATENGA CHIKHO CHACHITATU MU 2023
Timu yomwe yangolowa kumene mu TNM supa ligi ya Baka City tsopano yakwanitsa kutenga zikho zitatu mu chaka cha 2023 pomwe yakhala akatswiri a chikho cha Nyasa Capital Finance chakumpoto atagonjetsa Iponga FC 1-0 mu ndime yotsiriza lamulungu.
Eddie Mwangama anagoletsa chigoli chokhacho pa mphindi zinayi za masewero omwe kuti timuyi ikhale akatswiri.
Ichi ndi chikho chachitatu chaka chino atatenga Mayors Trophy Ku Tanzania my mwezi wa July komwe anagonjetsa matimu amu dzikoli ndipo atenganso ukatswiri wa ligi yakumpoto yomwe yawatengera mu Supa ligi.
The Clever Boys ikuyang'ananso zotenganso chachinayi pomwe akumane ndi Wanderers Reserve mu ndime ya matimu anayi mu King Kabvina Trophy ku Dowa.
BAKA CITY YALOWA MU SUPA LIGI
Timu ya Baka City yaku Karonga yakhala akatswiri a chikho cha SIMSO and Innobuild Northern Region Football League angakhale kuti kwatsala masewero awiri pomwe yagonjetsa Ekwendeni United 2-1 loweruka.
Timuyi yasewera masewero 12 mu ligiyi pomwe yapambana masewero 9 kufanana mphamvu kamodzi komanso kugonja kawiri kuti ipeze mapointsi 28 omwe palibe timu imene ingafikire mu ligiyi.
Timu ya Embangweni United ili pachiwiri ndi mapointsi 21, Kadona Stars ili pachitatu ndi 20 pointsi pomwe Iponga ili pachinayi ndi mapointsi 18. Mzimba United ndi Ekwendeni United ali pachisanu ndi pachisanu ndi chimodzi ndi mapointsi 16 pomwe Mayamiko Stars ili ndi mapointsi 9 ndipo Ekwendeni Hard Knockers ili ndi mapointsi 7.
Ngati matimu akumpoto onse a Moyale Barracks ndi Ekwendeni Hammers angapulumuke mu ligi, kukhala matimu asanu ku chigawochi.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
Baka eyes Super League promotion | Malawi 24 - Malawi news Karonga based Northern Region SIMSO Premier League side, Baka City FC, say they will leave no stone unturnedΒ to ensureΒ their objective of... malawi24.com