Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
"ANYAMATA AKUPHONYA KWAMBIRI" - MAKAWA
Mphunzitsi watimu ya Civo United, Abbas Makawa, wati kuchoka kwa Binwell Katinji kutimuyi kwapangitsa kuti asapeze anyamata odalilika ogoletsa zigoli ndi chifukwa chake akuphonya kwambiri mipata yochuluka.
Iye amayankhula atatha masewero omwe apambana 1-0 ndi timu ya FOMO pa bwalo la Civo ndipo wati anali masewero ovuta koma zilibwino poti apambana atagonja masewero atatu.
"Anali masewero ovuta kwambiri, timadziwa kuti avuta chifukwa anyamata ali ndi phuma kamba kophonya mipata komabe ndine okondwa poti tapambana. Mwina panopa tilibe katswiri wokhazikika oti azimwetsa zigoli, anachoka Binwell Katinji sitinapeze mlowammalo nde tiphunzitsabe omwe tili nawowa afikaponso." Anatero Makawa.
Timu ya Civo tsopano yafika pa nambala yachikhumi ndi chimodzi (11) pomwe yapambana kawiri ndi kugonja katatu ndipo ili ndi mapointsi asanu ndi imodzi (6).
"TIKUPHONYA MIPATA YOCHULUKA" - MAKAWA
Mphunzitsi watimu ya Civo United, Abbas Makawa, wati timu yake inaphonya mipata yochuluka yomwe yachititsa kuti agonje pomwe amakumana ndi Kamuzu Barracks.
Iye amayankhula atatha masewero omwe agonja 2-1 ndi timu ya KB ndipo wati timu yake inayesetsa kuti achite bwino koma wawamvetsetsa anyamata ake ndipo akonza.
"Anali masewero abwino kwambiri, tasewera bwino ndipo mipata tinayipeza koma chikusowa ndi kungogwetseramo mu golomo koma awanso ndi anthu, amakhala ndi zofooka ndipo tawamvetsetsa tikonza kuti tichite bwino mmasewero akudza." Anatero Makawa.
Iye anadandaulanso ndi kayimbilidwe ponena kuti oyimbira amapanga ziganizo zokomera KB ndipo iye sanakhutitsidwe nazo.
Timu ya Civo ili pa nambala 11 pomwe yatolera mapointsi atatu okha pa masewero anayi omwe yasewera.
"OMWE ANATISANGALATSA SABATA YATHA NDI OMWEWA" - MAKAWA
Mphunzitsi watimu ya Civo United, Abbas Makawa, wati akhale akuwalimbikitsa osewera ake kuti ayambirenso kuchita bwino poti ndi osewera ake omwewa omwe anapambananso sabata yatha.
Iye amayankhula atatha masewero omwe agonja 3-0 ndi Moyale Barracks pa bwalo la Mzuzu lero ndipo wati akonze monse molakwika kuti mmasewero ena azachitenso bwino.
"Lero zativuta tagonja kwambiri koma mwina tikanatha kupamba mu chigawo choyamba chomwe taphonya kwambiri koma zimachitika tiwalimbikitsa anyamatawa poti ndi omwewa omwe anatikondweretsa sabata yatha nde tiyesetsa." Anatero Makawa.
Timu ya Civo yayamba motsimphina mu ligi ya chaka chino pomwe yapambana masewero amodzi ndi kugonja awiri ndipo ali pa nambala yachisanu ndi chitatu (8).
"TIKUFUNIKA KUTI ALIYENSE AZIGOLETSA" - MAKAWA
Mphunzitsi watimu ya Civo United, Abbas Makawa, wati akulimbikitsa osewera ake onse kuti azikwanitsa kupeza zigoli ndi cholinga choti asamataye mipata yochuluka kuti azipambana masewero.
Iye amayankhula patsogolo pa masewero awo ndi Moyale Barracks kumathero a sabatayi pa bwalo la Mzuzu ndipo wati timu yake ikufunikira kukagoletsa zigoli zambiri kuti akapambane.
"Akhale masewero ovuta kutengera kuti tonse tili ndi ma pointsi atatu komanso kuti iwo ali pakwawo komabe takonzeka. Tikufunitsitsa kukapeza zigoli zambiri poti mumapambana ngati mukugoletsa nde titakagoletsa zambiri anzathu nkupeza mwina chimodzi ndekuti tikachita bwino nde tikufuna aliyense azitha kupeza zigoli ndekuti Civo ikondwa." Anatero Makawa.
Timuyi ili pa nambala yachisanu pomwe ili ndi mapointsi atatu pa masewero awiri ndipo masewero athawa inagonjetsa Dedza Dynamos 3-0.
"TINAYICHENJERERA DEDZA KUTI TICHITE BWINO" - MAKAWA
Mphunzitsi watimu ya Civo United, Abbas Makawa, wati chigoli cha msanga chinawathandiza kuti achite bwino ndipo ndi wokondwa kamba kopambana.
Iye amayankhula atatha masewero omwe apambana 3-0 ndi Dedza Dynamos ndi zigoli za Kelvin Kadzinje, Muhammad Biason komanso Emmanuel Savieli ndipo wati awalimbikitse osewera ake kuti azichitabe bwino.
"Anali masewero ovuta koma tinawachenjerera anzathuwa pomwe chigoli cha msanga chinatithandiza kwambiri kuwafoola koma tachita bwino, ku Mzuzu sabata yatha tinasewera bwino koma kuphonya nde lero tinawalimbikitsa, inde taphonya koma chipambano timachifuna Kwambiri." Anatero Makawa.
Timuyi tsopano ili pa nambala yachiwiri mu ligi ya TNM pomwe yatolera mapointsi atatu pa masewero awiri omwe yasewera.
CIVO YAKONZEKA KUKUMANA NDI DEDZA
Timu ya Civo United yati yakonzeka kukumana ndi Dedza Dynamos loweruka likudzali ndipo ikufunitsitsa itapeza chipambano kuti mitima ikhazikike kutimuyi.
Mphunzitsi watimuyi, Abbas Makawa, wati timu yake yamaliza zokonzekera zawo ndipo wati osewera Ake akudziwa kufunikira kopambana pakhomo ndikuti ayiwale kugonja Kwa sabata yatha ndi Mzuzu City Hammers.
"Tamaliza bwino zokonzekera ndipo zayenda bwino kwatsala ndi pabwalo, takonzekera kuti tikachite bwino chifukwa tinagonja mophweka sabata yatha pomwe tinamenya bwino koma sitinapeze chigoli nde mawa tigwira ntchito." Anatero Makawa.
Timu ya Civo inayamba moipa pomwe inagonja 1-0 ndi Mzuzu City Hammers yomwe inangokwanitsa kumenyera pagolo kamodzi kokha basi.
"WE MISSED A LOT OF CHANCES" - MAKAWA
Civo United head coach, Abbas Makawa, said his team missed a lot of chances and that cost them to suffer a defeat in Mzuzu.
Makawa said this after the team lost 1-0 to Mzuzu City Hammers at the Mzuzu Stadium on Sunday and said missed chances hurt the team.
"We played very well and controlled the game but we could not convert our chances and our friends got one chance and scored so we have rectify these problems so that we come out strong." Said Makawa.
The Servants sits 13th on the table after playing one game and have no point in the league.
MOSES BANDA NAMED AS CIVO CAPTAIN
Civo United has announced that midfielder, Moses Banda, is the new captain ahead of the 2024 season.
The announcement comes after Timothy Silwimba, who was the team's captain, moved to Mighty Mukuru Wanderers leaving the position void.
Meanwhile, he will be deputised by former Waka Waka Tigers captain, Masiya Manda and Righteous Banda in that order.
The team starts with an away match to Mzuzu City Hammers on Sunday in their league opener.
Reported by Hastings Wadza Kasonga Jr
CIVO YATENGA ATATU KU GREEN RANGERS
Timu ya Civo United yamalizitsa zotenga osewera atatu atimu ya Green Rangers, Yankho Biliati, Smey Chimunkho komanso Oscar Luwale omwe amayesa mwayi kutimuyi.
Timu ya Green Rangers yatsimikiza za nkhaniyi kudzera pa tsamba lake la Facebook ndipo yati osewerawa akhala akuyesa mwayi kwa miyezi iwiri ndipo Abbas Makawa wakhutira ndi ntchito za akatswiriwa.
Pa osewerawa, Billiat ndi Chimunkho amasewera kumbuyo pomwe Oscar Luwale walowa mmalo mwa Lloyd Aaron yemwe wapita ku FCB Nyasa Big Bullets.
Zonse zikatha, timu ya Civo ikhale ikutsimikiza kuti osewerawa asayina migwirizano wa miyezi yochuluka motani.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
CIVO BRING 10 NEW FACES
Capital City giants, Civo United, have made 10 new signings as they plan to build a strong team that will perform well in the 2024 season.
The Civil Servants has brought in 8 players who have been awarded three year contracts and two are signed on loan from FCB Nyasa Big Bullets.
The players are goalkeepers, Blessings Juma and Rahaman John, defenders Masiya Manda and Asimeyi Phiri, midfielders Righteous Banda and Simon Chimenya and strikers, Matthews Hamza and Foster Biton.
Meanwhile, the team's General Secretary, Edgar Chipalanjira, said the team will travel to Chipata in Zambia and Tete in Mozambique for friendlies ahead of the 2024 season.
The games will involve both men and Women senior teams as they want to feel the international football.
Timu ya Civo United yaonetsa makaka a malaya omwe atagwiritse ntchito mu ligi ya chaka cha 2024.
NEWS
Civo United's coach, Abbas Makawa, has penned a three year contract to stay at the team.
He took charge of the team last season as an interim and rescued them from relegation as well as securing a top 8 finish.
SIGNED
Civo United has confirmed the signing of defender, Masiya Manda, from Mighty Wakawaka Tigers.
He has signed a three year contract with the Civil servants.
CONFIRMED
Civo united has confirmed the signing of forward, Mphatso Magaleta, who has joined from FCB Nyasa Big Bullets for a period of one year on loan.
CONFIRMED!
Civo United has signed striker Emmanuel Savieli, on loan from FCB Nyasa Big Bullets for a period of one year.
CIVO SIGNS MANDA
In a bid to strengthen their squad in the 2024 season, Civo United has signed Mighty Tigers captain, Masiya Manda, who has already penned his contract, our sources have confirmed.
Manda has confirmed the news to one of his friends at Tigers who has informed us about the news and that he will be unveiled anyday from tomorrow.
Meanwhile, the team has also roped in Mphatso Magaleta and Emmanuel Savieli, who have signed a one year loan contract from FCB Nyasa Big Bullets.
These three players will make it five in total as new signatures for the Civil Servants and that is putting them as one of the teams to have a strong squad in 2024 and maybe contenders for the TNM Super League championship.
1. Blessings Juma 2. Rahaman John 3. Mphatso Magaleta 4. Emmanuel Savieli 5. Masiya Manda
According to Edgar Chipalanjira, who is the teams General secretary, the team is left to sign a defender, a midfielder and a striker. All three signed players will be unveiled on Monday.
CIVO YATENGA JUMA
Timu ya Civo United yalengeza kuti yatenga goloboyi watimu wa Extreme FC, Blessings Juma, kuti akatumikire kutimuyi.
Juma wasaina mgwirizano wa zaka zitatu ndi timuyi ndipo akhalebe kutimuyi mpaka mu 2027.
CIVO SIGN JOHN
Civo Service Football Club has signed the goalkeeper who has been released by FCB Nyasa Big Bullets earlier this month, Rahaman John, as a free agent.
The player has penned a three year deal after completing all necessary document to play for the Capital city giants.
He played for Bangwe All Stars last season where he was one of the two goalkeepers to score a goal which netted against Civo United at the Civo Stadium.
Meanwhile, the team will announce the deal soon as they also eye to sign another goalkeeper, with Blessings Juma, being the one rumored for the move.
Source: Twaha Chimuka
TRANSFER NEWS
Civo United has agreed personal terms with Extreme FC goalkeeper, Blessings Juma, and that the goalkeeper will join the Civil Servants.
The Servants has beaten Dedza Dynamos and Bangwe All Stars as they plan to give him an outline deal.
HARRY NYIRENDA NDI ENA ACHOTSEDWA KU CIVO
Team ya Civil Service United FC yachotsa osewela asanu ndi awiri pomwe ikufuna kuyamba zokomzekera zawo.
Malingana ndi mlembi wa team ya Civil, Edgar Chipalanjira wauza wayilesi ya Kasupe mmawa wa lachinayi kuti ndizoona achotsadi anyamatawa omwe alipo 7.
Osewelawa ndi Luke Chima, William Bwetu Mwalwimba, Harry Nyirenda, Frank Banda, Sugzo Mwakasinga, Dan Kumwenda ndi Innocent Tanganyika.
Chipalanjira wati osewera Innocent Tanganyika akhale akuthandiza team yachisodzela ya Civil.
Posachedwapa, mlembi wa Civil adaululaso kuti osewera wawo Lloyd Banega Aaron akhale akulowela ku team ya FCB Nyasa Big Bullets.
Wolemba : Gift Tembo