Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
"TIKANATHA KUGOLETSANSO ZINA ZAMBIRI" - BUNYA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Andrew Bunya, wati timu yake ikhazikika pa chidwi chogwiritsa ntchito kwambiri mipata yomwe anayipeza mchifukwa chake akwanitsa kupambana masewero awo oyamba mu 2024.
Iye amayankhula atatha masewero omwe apambana 3-0 ndi timu ya MAFCO pa zigoli zomwe zinafika mchigawo choyamba ndipo wati timu yake ikanathanso kupeza zochuluka kuposa zimenezi.
"Anali masewero ovuta ndipo timadziwa kuti avuta chifukwa anzathunso amafuna kupambana koma tinangosamala kuti tipeze mipata yochuluka ndipo tiyigwiritse ntchito, ndithokoze anyamata anakwanitsa kutero koma tikanathanso kupeza mipata yambiri." Anatero Bunya.
Iye wati chipambano chimenechi chipereke mphamvu kutimu poti tsopano anyamuka mu ulendo wawo wofuna kuchita bwino mu 2024.
Timuyi ili ndi mapointsi asanu ndi imodzi (6) pomwe yagonja kamodzi, kufanana mphamvu katatu ndi kupambana kamodzinso ndipo ali pa nambala Khumi.
"TIKUFUNIKA KUKONZA KUMBALI YOGOLETSA" - BUNYA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Andrew Bunya, wati timu yake ili ndi ntchito yokonza kutsogolo kwawo ngati akufunikira kuti ayambe kupezanso zipambano mu ligi ya TNM.
Iye amayankhula patsogolo pa masewero awo ndi MAFCO pa bwalo la Dedza lamulungu ndipotu wati anyamata ake akusewera bwino ndipo akangokwanitsa kumagoletsa ndekuti zipambano ziwapeza.
"Masewero apita aja mipata tinayipeza yochuluka kwambiri koma kuti tigoletse kukanika, timatha kupita kutsogolo komanso kupangitsa kuti anzathu alakwitse kumbuyo kwawo koma kuti mpira ugunde ukonde ukamanika nde tikonza mbali imeneyo zimatheka tiyambanso kuchita bwino." Anatero Bunya.
Timuyi ikupita mmasewerowa ikusaka chipambano chawo choyamba pomwe yagonja kamodzi ndi kufanana mphamvu katatu kuti akhale ndi mapointsi atatu pa masewero anayi pa nambala 12.
Premier Bet sweetens Dedza Dynamos
Premier Bet company and TNM Super League side Dedza Dynamos have signed a sponsorship agreement worth K100 million until the end of the season with an option to extend.
The signing ceremony took place today at Premier Bet Offices in Limbe,Blantyre.
As part of the sponsorship agreement ,the team will now be called Premier Bet Dedza Dynamos FC.
Inside the deal, MK100,000 will be provided to the player of the month until the end of the season, Player of the year will get MK500,000, Fan player of the year will also get MK500,000 and the supporter of the year will get MK200,000 as well.
"OYIMBIRA SANAGWIRE BWINO NTCHITO" - BUNYA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Andrew Bunya, wati kupatula kuphonya mipata yawo, oyimbira sanagwire bwino ntchito yake zomwe zachititsa kuti asapeze chigoli.
Iye amayankhula atatha masewero omwe afanana mphamvu 0-0 ndi Moyale Barracks ndipo wati sakudziwa kuti kunali kukondera kapena kusadziwa ntchito koma oyimbira wakanika kugwira ntchito yake.
"Tinakonza kuti mchigawo choyamba tiwasunge koma mchigawo chachiwiri tipite kutsogolo kwambiri nde koma mipata tinayipeza tinaphonya koma ina timagwetsedwa mu box koma oyimbira sanafune kuyimba, osati kuti timafuna kukonderedwa koma ntchito yawavuta." Anatero Bunya.
Timu ya Dedza Dynamos ili pa nambala 13 mu ligi pomwe ili ndi mapointsi atatu pomwe yafanana mphamvu katatu ndi kugonja kamodzi.
"WE ARE FACING A FREE SCORING MOYALE" - BUNYA
Dedza Dynamos head coach, Andrew Bunya, said his team needs to be strong in defense as they face Moyale Barracks which a joint most scoring team in the TNM Super League after three weeks.
Bunya said this ahead of meeting the Lions of Kaning'ina at Mzuzu Stadium on Sunday and said his team needs to record a win against Moyale so that they have strengths in their forthcoming matches.
"We are capable of doing more than what we have done as of now going into the fourth week of the season. We're facing a team that has managed to score goals in all their games played so far and it means that we have to be strong enough at the back." Said Bunya.
He further said everyone at the team has to be committed so that they achieve better results in their matches this season. He said Edward Dakalira is out due to injury whereas Samson Tijani will still miss due to paperwork.
Dedza Dynamos FC sits on position 14 with two points managing two draws and a
"IT'S A PAINFUL RESULT FOR US" - BUNYA
Dedza Dynamos coach, Andrew Bunya, said a draw against Silver Strikers was a heartbreaking result for his side as he was targeting a win in the match.
He said this after held by the Bankers to a 1-1 draw at the Dedza Stadium and told the supporters to remain calm as the team is under rehabilitation.
"It's a bad result for us as we prepared for a win. We started well and got that goal but in the second half, Silver attacked us and we failed to contain them of which the got a goal then we attacked them again and I thought we could have a penalty but the referee thought it otherwise." Said Bunya.
He said he is confident that the team will do better in the coming games as it has shown some positives in the game.
The team sits 14th on the table after failing to pick a win in the league and have two points from their three games this season.
"ANALI MASEWERO OVUTA KWAMBIRI" - BUNYA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Andrew Bunya, wati timu yake inayilora Civo kuti ipatsirane kwambiri mchifukwa chake sinakwanitse kuyigwira mpaka agonja.
Iye amayankhula atatha masewero omwe agonja 3-0 ndi Civo ndipo wati kutsegula komwe anachita mchigawo chachiwiri kunangowaputira nkhondo pomwe anapezetsa chigoli chachiwiri.
"Anali masewero ovuta kwambiri kutengera kuti tonse sitimachokera ku zotsatira zabwino koma tinawalora anzathu kukhala ndi mpira zomwe zinawapatsa mpata kuti apeze chigoli. Mchigawo chachiwiri tinasintha kuti tipanikize koma anagoletsa zomwe zinawafoola anyamata." Anatero Bunya.
Timuyi ikumane ndi Silver Strikers mmasewero awo otsatira ndipo ili ndi point imodzi pa nambala 13 pa masewero awiri mu ligi.
Dedza 2-1 fcb nyasa bb
"BEATING BULLETS IS A MORALE BOOSTER" - BUNYA
Dedza Dynamos head coach, Andrew Bunya, said his team is ready to face FCB Nyasa Big Bullets and a victory will help to build confidence to compete in the 2024 TNM Super League season.
Bunya said this ahead of the two teams meeting at the Dedza Stadium in the leagues opener and said what was lacking during the Pre-Season has been fine tuned for the betterment of the season.
"We have finalised our trainings and I would say we are good to go, the boys have assured me that they are ready and I'm assured that they are physically fit and also mentally fit so against Bullets we just have to apply these." Said Bunya.
Meanwhile, the coach said the team was struggling to find goals up front but they have sorted out the problem and will make sure to start with the win to set themselves ready to compete for trophies this season.
Dedza Dynamos is playing its third season in the top flight leagues and have finished in the top 8 in both campaigns as
DYNAMOS CATCH A NIGERIAN STRIKER
Dedza Dynamos FC has announced the signing of Nigerian striker Samson Olatubosun Tijani who has penned a two-year deal on Monday.
The 20-year-old striker previously played for A.A AZTEC football academy in Nigeria and he has impressed the technical panel in the two weeks he has been training with the team.
Speaking to the team's media after completing his move, Tijani said his dream has come true as he has been looking for an opportunity in Malawi.
"I thank God for making my dream a reality and I can't wait to start my journey with this ambitious club. I am happy that they have trusted me and I will pay back that trust on the field of play with goals," Tijani indicated.
Dedza Dynamos play FCB Nyasa Big Bullets in their 2024 TNM Super League opener on Saturday and has lost their two prolific strikers, Charles Chipala and Clement Nyondo to Silver Strikers and Mighty Wanderers Respectively.
📷: Dedza Dynamos media
Masapota a Dedza Dynamos akusemphana!
Pali chimkulirano komanso kusamvana maganizo pakati pa masapota atimu ya Dedza Dynamos pomwe ena asakugwirizana ndi kuti Andrew Bunya atsogolere timuyi mu 2024.
Mphunzitsiyu yemwe walowa mmalo mwa Gilbert Chirwa ndipo kwawo ndi ku Dedza komweko wayang'anilidwa mmaso ndi ena mwa masapota omwe akuti iye ayitulutsitsa mu ligi ya TNM.
Koma gulu lina la masapotawa ali okwiya ndi zoyankhula za enawa pomwe akuti Bunya ndi mphunzitsi wabwino ndipo akungomukana poti akumudziwa.
Mphunzitsiyu anaphunzitsapo Extreme FC kumapetopeto Kwa masewero awo mu 2023.
DEDZA YASAINA CHIKUFENJI
Timu ya Dedza Dynamos yalengeza kuti yasaina katswiri wosewera kumbuyo kapenanso pakati watimu ya Mighty Tigers, Frank Chikufenji, yemwe wasaina mgwirizano wa zaka ziwiri ku Mbatatesiku.
Iye wapita kutimuyi mwaulere kutsatira kutha kwa mgwirizano wake ndipo wati wakondwa kamba kopita kutimuyi.
"Ndine wosangalala poti ndasaina ndi timu yabwino yatsogolo ngati iyi ndipo ndikuona kuchedwa kuti ndiyambe kugwira ntchito pa bwalo. Dedza yakhala timu yakumaloto kwanga angakhale tikamakumana nayo ndipo lero zatheka." Anatero Chikufenji.
Ndipo mlembi wamkulu watimuyi, Kondwani Banda, wati ichi ndi chiyambi chokunga timu yamphamvu yoti ichite bwino ndipo ikhala ikusainanso osewera ena mmasiku akubwerawa.
Timuyi inathera pa nambala yachisanu ndi chiwiri ligi cha chaka chatha ndipo iyamba zokonzekera zawo lolemba likudzali.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
"SINDINGAYANKHULEPO ZAMBIRI KUTI NDICHOKA" - NYONDO
Wosewera mbambande womwetsa zigoli kutimu ya Dedza Dynamos, Clement Nyondo, wati ndi wokondwa kamba kopambana mphoto ya wosewera womwetsa zigoli zambiri mu ligi ndipo wati alimbikirabe kuti chaka cha mawa adzachitenso bwino.
Iye amayankhula atatha masewero omwe timu yake yagonja 2-1 ndipo anagoletsa chigoli pa penate kuti zikwane 16 ndi kutenga mphotoyi. Iye wathokoza osewera anzake pomuthandiza kuti atenge mphotoyi.
"Ndine wokondwa kwambiri kuti ndapambana mphotoyi, sizinali zophweka koma ndinalimbikira kwambiri. Ndilimbikirabe kuti chaka cha mawa ndizachite bwino ndipo ndithokoze anzanga pondithandiza kuti ndapambane. Zoti ndichoka sindingayankhule zambiri poti sindikudziwa za mtsogolo." Anatero Nyondo.
Nyondo wamaliza ndi zigoli 16, ziwiri pamwamba pa katswiri wa FCB Nyasa Big Bullets, Lanjesi Nkhoma ndipo aka ndi koyamba kugoletsa zigoli zambiri kotere.
"IFE NGATI DEDZA TATHERA PABWINO" - CHIRWA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Gilbert Chirwa, wati timu yake yathera pabwino mu ligi ya TNM angakhale kuti anthu amawadelera kuti sangachite bwino.
Iye amayankhula atatha masewero omwe agonja 2-1 ndi Ekwendeni Hammers pa bwalo la Rumphi ndipo anati Ekwendeni inabwera mwamphamvu kwambiri komabe ndiwokondwa kuti athera pa nambala yabwino.
"Anali masewero ovuta kwambiri anzathuwa anatipanikiza kwambiri mwina poti anali pa ngozi nde tinachinyitsa zigoli ziwiri koma chigawo chachiwiri tinasewera bwino mpaka tinapeza chigoli koma tathera pa nambala 7 ndipo tonse takondwa kwambiri." Anatero Chirwa.
Timu ya Dedza Dynamos yathera pa nambala yachisanu ndi chiwiri (7) pomwe yatolera mapointsi okwana 38 pa masewero 30 omwe yasewera.
"TITHOKOZE ANYAMATA POTI ANALIMBIKIRA" - CHIRWA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Gilbert Chirwa, wayamikira anyamata ake kamba kochilimika mpaka kugonjetsa timu ya FCB Nyasa Big Bullets ndipo wati anakambirana zoti ayidzidzimutse Bullets.
Iye amayankhula izi atagonjetsa FCB Nyasa Big Bullets 1-0 pa bwalo la Dedza ndi chigoli cha Clement Nyondo mu mphindi yoyamba ndipo wati anyamata ake agwira ntchito yotamandika.
"Analidi masewero ovuta kwambiri koma anyamata anachilimika, anatsatira chimene timawauza kuti Bullets imapita kwambiri kutsogolo nde titseke mipata yonse nde anyamata apanga zimene tinawauza komanso tinakambirana kuti tidzidzimutse Bullets." Anatero Chirwa.
Timuyi ili pa nambala yachisanu ndi chitatu (8) pa masewero 29 omwe yasewera ndi mapointsi 38 ndipo yatsala ndi masewero amodzi kuti amalize ligi ya chaka chino.
"ONE OF THEIR PLAYERS WERE OFFSIDE" - CHIRWA
Dedza Dynamos head coach, Gilbert Chirwa, says the referee could have denied the Ekwendeni Hammers' equaliser in their match as one of the players was offside.
Chirwa said this after the match which his team lost 6-5 on penalties after a 1-1 draw in the regulation time and blamed the officiation for awarding the goal but says they will switch attention to their next game against FCB Nyasa Big Bullets.
"The game was good and we were leading 1+0 and Ekwendeni equalised through a free kick but I think one of their players was completely offside and the whole bench was surprised as to why they did not raise the flag otherwise penalties are unpredictable, they won." Said Chirwa.
Christopher Phiri netted an opener on 16th minute via a penalty but Chisomo Sambani's header on 65th minute forced the game into the penalty where Charles Chipala's miss gifted Hammers a win.
The team turns attention to the league where they will play FCB Nyasa Big
NYONDO AND CHIPALA FIT FOR GAMES AT DEDZA DYNAMOS
Dedza Dynamos has received a major boost in their upcoming matches after their two prolific forwards, Clement Nyondo and Charles Chipala, return to the pitch as they have recovered from their injuries.
The team will play the Castel Challenge Cup round of 16 match against Ekwendeni Hammers on Sunday before winding up their two TNM Super league fixtures and coach, Gilbert Chirwa believes his team could finish strong with the recent developments.
"We were hit hard by injuries to our strikers and their return is a big boost to the team ahead of our final games this season," Chirwa said to the team's media crew.
He further said the team's current performance isn't that pleasing but they will try to finish the season on high.
"We understand the frustrations from our fans and they should understand that no one is happy with our performance including us and the players but every challenge comes up with a success story," Chirwa explained.
Dedza Dynamos looking from far from an eye of a common person, seems to be a great team. Guess their performance will keep on improving.
https://shorturl.at/joV07
"PENANSO OYIMBIRAWA AMATHANDIZA ANZATHUWA" - CHIRWA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Gilbert Chirwa, wati wavomereza kugonja poti timu yake inapereketsa zigoli zophweka kwambiri koma wati oyimbira anaithandizakonso Bangwe All Stars.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe agonja 3-0 pa bwalo la Mpira ndipo wati ziganizo zina zimasemphana ndi mmene zimafunikira komabe mavuto awo akonza.
"Inde chabwino tagonja koma pena tizinena chilungamo oyimbirawa ah pena ziganizo zawo zinali zokomera anzathuwa, ma offside awo samayimba komanso ma free kick omwe amawapeza anali abodza koma tavomereza, ndi Wanderers sitizabwereza zolakwa zathu." Anatero Chirwa.
Timuyi tsopano yatsika kufika pa nambala yachisanu ndi chitatu (8) pomwe ili ndi mapointsi 35 pa masewero 26 omwe yasewera mu ligiyi.
#KasongaJr
"TIMU IKAGONJA SIKUTI IZINGOGONJABE" - CHIRWA
Mphunzitsi watimu ya Dedza Dynamos, Gilbert Chirwa, wadzudzula mchitidwe wa anthu omwe akumayankhula kwambiri timuyi ikapanda kuchita bwino pomwe wati mu mpira matimu amaluzanso.
Iye amayankhula izi atagonjetsa timu ya Blue Eagles 2-1 pa bwalo la Dedza ndipo wati masewero awo anali ovuta koma chipambano chinali chofunika potseka pakamwa anthu oyankhula kwambiri.
"Vuto lake anthu amayankhula kwambiri, ineyo ndamenyapo mpira, nthawi zonse sikuti mukaluza ndekuti ndinu oluza basi nde komabe anyamata anaikapo mtima lero kuchokera kumbuyo mpaka tapambana." Anatero Chirwa.
Chipambano cha timuyi chaitengera pa nambala yachisanu ndi chimodzi (6) pomwe ali ndi mapointsi 34 pa masewero 24 omwe yasewera mu ligiyi.
#Tawonga2023