Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
"TIKUFUNA TISAMATAYE MA POINTSI PAKHOMO" - MWANSA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Prichard Mwansa, wati ndi wokondwa kamba koti timu yake yapeza chipambano chawo chachiwiri mu ligi ya TNM ya chaka chino ndipo wati akufuna kuti azichita bwino masewero apakhomo.
Iye amayankhula atatha masewero omwe apambana 3-0 ndi timu ya Civo United ndipo wati salekera pomwepa pomwe alimbikitse osewera ake kuti azichita bwino.
"Tasewera bwino kwambiri ndipo tapambana masewerowa anyamata anachita bwino ndipo timafunitsitsa kupambana uku poti timachoka kogonja nde zakhala bwino poti tikufunitsitsa kuti masewero apakhomo tizichita bwino kuti kwa Ife tikhale tilibwino." Anatero Mwansa.
Timu ya Moyale tsopano yafika pa nambala yachitatu mu ligi pomwe ili ndi mapointsi asanu ndi imodzi (6) pa masewero atatu omwe yasewera mu ligi.
"ITS A MUST WIN GAME FOR US" - MWANSA
Moyale Barracks head coach, Pritchard Mwansa, says their match against Civo United on Saturday is a must win as they look to pick up from the positive result of the game.
Mwansa said this ahead of the match at the Mzuzu Stadium and said he has prepared his team to defend well after found to concede four goals in their opening two games.
"It is a tough game looking at how our friends are, they are a good team but we are prepared and have solved every problem encountered in the past two games so this is a must win for us so that we pick up from that win going ahead in the league." Said Mwansa.
The former Moyale Barracks midfielder said his team will look to defend more and attack more in the same process as they look to pick a win in the match.
Moyale are 7th on the table after collecting three points from two games they have played so far in the 2024 TNM Super League season.
MWANSA TO RELEASE MOYALE FINAL SQUAD ON TUESDAY
Moyale Barracks has announced that their coach, Pritchard Mwansa, will release the team's squad for the 2024 season on Tuesday, 02nd March 2024.
The team made the announcement via their Facebook page with confirmation that the coach will stay at Moyale despite MAFCO's announcement that he will lead them.
"Moyale Barracks football team Coach, Prichard Mwansa will release the 2024 Final Squad on Tuesday 2 April, 2024 at Exactly 12 midday." The report read.
The team survived relegation last season after beating Red Lions 7-0 on the final day and had its two veterans, Macdonald Harawa and Gastin Simkonda retiring from Football.
DEAL DONE!
Moyale Barracks has announced the signing of defender, Peter Ng'ambi from Iponga FC.
He is the third signing of the team since yesterday.
NEW SIGNING
Moyale Barracks has also announced the signing of a 20 year old midfielder, Jimmy Viyuyi.
The young talent was playing for Karonga United Reserve before heading to Kaning'ina.
NEWS
Moyale Barracks has announced the signing of a 21 years old Striker, Emmanuel Allan, from Changalume Barracks Striker.
Moyale Barracks Football Club Elect New Supporter's Committee
Moyale Barracks football club supporters on Tuesday went into Electoral General Meeting to elect new committee members
The new Supporter's committee started working with immediate effect from Wednesday March 20, 2024.
67 Supporters came to elect the new committee that took place at Mzuzu Stadium.
Owen Banda elected as New Chairperson and below are the full elected list.
Chairperson - Owen cChikafumbwa Banda Vice Chair - Richard Mengwa General Secretary - Pearson Kang'ombe Vice - Marcus Shengwayo Treasure - Zikomo Kapichi
Committee Members 1, MacDonald Chunga 2, Magret Chiumia Discipline Members 1, Baton Nyondo 2, AP Nyirenda
MEDHEALTH DIVORCES MOYALE BARRACKS
Moyale Barracks' kit Sponsors, Medhealth have parted ways with the team after the expiry of contract on Tuesday, the team has confirmed.
In a press release signed by the General Secretary, Lt. Omega Masamba, confirmed about the divorce and thanked the company for assisting them in the past three years.
"Moyale Barracks Sports wishes to notify all media outlets and the general public that our partnership with Medhealth as the Jersey Sponsors concluded at the end of February 2024, with no plans for renewal after three years of collaboration." Reads the part of the release.
Meanwhile, the team appeals to all companies and sponsors that are willing to assist them to do so that they can move well in the 2024 season.
The Lions of Kaning'ina survived relegation on the very last day of the league following a 7-0 win over Red Lions last season.
"NDINE WOKONDWA NDI MMENE ANYAMATA AKUSEWERERA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati ndi wokondwa ndi mmene timu yake ikusewerera koma wafunira zabwino timu ya Mighty Mukuru Wanderers pomwe ikupitilira mu Chikho cha Castel.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe anagonja 3-0 ndi Manoma pa bwalo la Kamuzu ndipo wati kumbuyo kwa timuyi ndi kumene kunavuta mmasewerowa.
"Anali masewero abwino kwambiri, tinasewera bwino kwambiri ndipo ndine okondwa ndi mmene anyamata akusewerera pano koma mwina mphindi zisanu zakumapeto mchigawo choyamba kumbuyo kwathu kunagona koma zimachitika mu mpira tingoifunira zabwino Wanderers." Anatero Chingoka.
Timuyi tsopano yamaliza masewero ake a chaka cha 2023 ndipo akuyembekeza kukapumira kukonzekera ligi ya chaka cha 2024 pomwe anapulumuka pa tsiku lotsiliza lenileni mu ligi.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
"SIKUTI LINALI PHWANDO NAYO RED LIONS IMASEWERA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati kupambana 7-0 ndi timu ya Red Lions sinali phwando kapena kupatsidwa koma wati ndi okondwa poti timuyi yatsala mu ligi.
Iye amayankhula atatha masewerowa omwe Gastin Simkonda anamwetsa zigoli zinayi, Raphael Phiri ziwiri ndi George Nyirenda chimodzi ndipo wati timu yake inasewera bwino kwambiri.
"Anali masewero abwino kwambiri lero anyamata anapita kutsogolo kwambiri nde zatithandiza kuti tipeze zigoli ndipo kumapetoku anyamata akulimbikira kwambiri nde ndine wokondwa kuti tatsalabe mu ligi. Sikuti linali phwando ayi chifukwa Red Lions nayonso imasewera bwino koma ikafika kutsogolo imaphonya kwambiri." Anatero Chingoka.
Timu ya Moyale yatsala mu ligi kamba koti inatenga mapointsi ambiri pa Blue Eagles yomwe anafanana nayo kalikonse ndipo yathera pa nambala 13 ndi mapointsi 35.
"TSOPANO NDIKUDERA NKHAWA NDIPO NDILI NDI MANTHA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks wati ali ndi mantha tsopano ndi tsogolo la timuyi mu ligi ya TNM pomwe wati masewero awo ndi MAFCO amayenera kupambana.
Iye amayankhula atatha masewero omwe analepherana 1-1 pa bwalo la Mzuzu ndipo wati oyimbira wawakanira zigoli ziwiri zoonekeratu koma kufanana mphamvuku kwapereka mantha kwa iyeyo.
"Pakadali pano ndili ndi mantha kwambiri ndipo ndikudera nkhawa chifukwa timayenera kupambana mmasewero awawa koma tsopano sindikudziwa kuti mmasewero ena akubwerawa anzathu amaliza motani." Anatero Chingoka.
Timu ya Moyale ili ndi mapointsi 32 pa masewero 29 pa nambala 14 ndipo ikuyenera kukumana ndi timu ya Red Lions yomwe inatuluka kale mu masewero awo omaliza amu ligi ya TNM.
"NDIKUKHULUPILIRA KUTI MOYALE SITULUKA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati timu yake sikutuluka mu ligi ndipo ayesetsa kuti amalize bwino mmasewero awo omwe atsala nawo kuti ligi ya chaka cha mawa adzayambire pamenepo.
Iye amayankhula izi patsogolo pa masewero awo ndi MAFCO loweruka ndipo wati akudziwa kuti akhala masewero ovuta kutengera kuti matimu onse ali pa ngozi yotuluka mu ligi ngati sachita bwino.
"Kukonzekera kwathu takonzekera monga mwa nthawi zonse komabe tikudziwa kuti masewero akhala ovuta chifukwa anzathuwa abweranso kuti asunge malo amu ligi komabe ifeyo tikufunitsitsa kuti timalize bwino kuti chaka cha mawa tidzayambire pamenepo. Moyale sikutuluka mu ligi." Anatero Chingoka.
Timu ya Moyale ili pa nambala yachikhumi ndi chinayi (14) pomwe ili ndi mapointsi 31 pa masewero 28 omwe yasewera mu ligiyi.
"OSEWERA ATHU AWIRI APITA NAWO KU CHIPATALA" - SIMKONDA
Mtsogoleri wa osewera atimu ya Moyale Barracks, Gastin Simkonda, wati timu yawo sinyamuka lero kumapita ku Mzuzu kuti amakonzekere za masewero awo ndi FCB Nyasa Big Bullets pomwe wati sangayende bus yawo ili yosweka.
Iye amayankhula izi kutsatira kuphwanyidwa kwa galimoto yomwe amayendera ndi anthu aku Dedza pomwe timuyi inalepherana 1-1 ndi Dedza Dynamos ndipo wati zimenezi si zampira pomwe Chifundo Damba ndi Timothy Nyirenda onse avulazidwa.
"Timalimbikira zokonzekera kuti tizichita bwino komanso pa bwalo la zamasewero timalimbikiranso koma oyimbira akumatisokoneza lero awapatsa penate yabodzanso chabwino tayivomera kenako akutigenda ndi kutiphwanyira bus yathu mpaka anzathu awiri athamanga nawo ku chipatala." Anatero Simkonda.
Iye wati ndi zovuta kuyenda kamba ka mphepo ndi zinthu zina ndipo wati si zampira. Mkulirano unabuka pomwe osewera a Moyale amafuna kumugwira nthupi oyimbira kamba ka penate yomwe anaipatsa Dedza Dyna
"MWINA AMAPHWEKETSA TIGERS POTI TINAIMITSA WANDERERS" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati ndi wokhumudwa kwambiri ndi mmene timu yake inasewera lachitatu pa bwalo la Kamuzu ndipo wati waonera mpira woipa chiyambireni ku timuyi.
Iye wayankhula izi atatha masewero omwe agonja 3-0 ndi Tigers ndipo wati mwina kuiderera Tigers ndi kumene kwawapweteketsa poti amachoka koimitsa Wanderers.
"Sitinasewere bwino ndipo sindinasangalatsidwe, mwina anatayilira poti anasewera bwino ndi Wanderers koma kaseweredwe akaka ndi koipitsitsa komwe ine ndaonako, ndakhumudwa kwambiri, zimachitika koma osati ndi zigoli zonsezi." Anatero Chingoka.
Iye wati akonza mavuto awo kuti akamakumana ndi Bullets adzachite bwino ndipo osewera awo ovulala awagwiragwiranso kuti adzapezeke. Moyale ili pa nambala 12 ndi mapointsi 30 pa masewero 25.
#Tawonga2023
"KUMBUYO KWA WANDERERS SAMAYENDA NDE TINAPEZA MPATA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati kufanana mphamvu koyenda ndi timu ya Wanderers ndi zonyaditsa ndipo ziwathandizira pa nkhondo yawo yotsala mu ligi.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe anapeza chigoli mu mphindi zakumapeto kuti afanane mphamvu 1-1 ndipo wati anayiona Wanderers chofooka chomwe osewera ake anagwiritsa ntchito.
"Ndinayiona kuti Wanderers sikuyenda kumbuyo kwawo nde ndinawauza osewera kuti ayipanikizebe mchigawo chawo chomwecho mpaka zinatheka kuti tapeza chigoli chomwe ndi chofunikira kwambiri." Anatero Chingoka.
Moyale tsopano izipita mmasewero awo ndi Mighty Wakawaka Tigers lachitatuli ili pa nambala 11 ndi mapointsi 30 pa masewero 24.
"SITILI PA MTENDERE NDIPO TIKUFUNIKA KUCHILIMIKA" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati ndi wokondwa kwambiri kamba koti timu yake yapeza chipambano pomwe amasewera ndi Civo United koma wati sizikutanthauza kuti ali pa mtendere.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe apambana 1-0 pa bwalo la Rumphi ndipo wati samayembekezera kuti timuyi ingasewere bwino motero.
"Ndine wosangalala kwambiri Chimwemwe chodzadza tsaya komanso ndiwanyadire osewera athu sindimayembekezera kuti tingapambane poti anyamata ambiri ndi ovulala koma asewera bwino. Tichilimikabe chifukwa ligi yavuta nde pakufunika osamataya mapointsi." Anatero Chingoka.
Moyale tsopano yafika pa nambala 11 pomwe yatolera mapointsi 29 pa masewero 23 omwe yasewera mu ligiyi.
"KUTENGA LIGI KUTIVUTA KOMA KUKHALABE MULIGIMU" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati wauza osewera ake kuti asagone chifukwa choti atuluka ku malo a matimu otuluka mu ligi koma akuyenera kuchilimbika kwambiri poti sali otetezekabe.
Iye amayankhula izi kutsatira kupambana 2-0 ndi timu ya Extreme FC pa bwalo la Nankhaka ndipo wati ndi okondwa kamba ka chipambanochi. Iye wapempha osewera ake kuti achilimike kuti akhalebe mu ligiyi.
"Mukuona mmene ligi yavutiramu sitili pabwinobe nde tawauza osewera kuti apeze zipambano mwina mmasewero atatu kapena anayi zimenezi zitha kutikhalira bwino." Anatero Chingoka.
Iye wati vuto lalikulu lili komwetsa zigoli ndipo ayesetsa kukonza zinthuzi kuti izipeza zigoli. Moyale yafika pa nambala 11 pomwe ili ndi mapointsi 26 mmasewero 22 omwe asewera.
"ZIVUTE ZITANI MAWA TIKUSWA EXTREME" - CHINGOKA
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Victor Chingoka, wati timu yake yakonzekera kuti apeze chipambano mmasewero awo ndi Extreme FC pomwe akufuna kuchoka ku chigwa cha matimu otuluka mu ligi ya TNM.
Iye wayankhula izi patsogolo pa masewerowa omwe alipo pa bwalo la Nankhaka ndipo wati mavuto omwe anali nawo okanika kugoletsa zigoli awakonza ndipo akonzeka kutchisa Fodya waku Mchinji.
"Takonza mmene timakonzekerera masewero aliwonse koma awawa tipita ndi cholinga kwambiri chifukwa sizikutiyendera mu ligi. Chomwe chimativuta ndi kupeza zigoli nde ndi zimene taunikirapo kwambiri ndipo anyamata tawauza kuti mwa njira iliyonse tikapambane. Extreme nayo ilinso kumunsi nde sibwera mwachibwana komabe tiyesetsa kuti tipambane." Anatero Chingoka.
Awa akhala masewero oyamba ngati mphunzitsi watimuyi a Chingoka ndipo ngati angapambane, iwo atuluka mu munsi kwa ligiyi. Moyale ili ndi mapointsi 23 pa nambala 14.
BREAKING
Timu ya Moyale Barracks yaimitsa ntchito mphunzitsi, Nicolas Mhango, kamba ka kusachita bwino kwa timuyi.
Izi zadziwika pa mkumano umene timuyi inali nawo yowunikira mmene timuyi ikuchitira komanso zifukwa zimene isakuchitira bwino.
Padakali pano, Victor Chingoka, yemwe ndi wachiwiri kwa Mhango, atsogolera timuyi pomwe ikukumana ndi Extreme FC loweruka pa bwalo la Nankhaka.
Mhango anatulutsa kale Bangwe All Stars mu chigawo choyamba ndipo ili pa nambala yachisanu ndi chiwiri (7) pomwe Moyale ili pa nambala 14 ndi mapointsi 23.
Source: VOL
"OYIMBIRA ANATIBALALITSA NDE TAGONJA" - MHANGO
Mphunzitsi watimu ya Moyale Barracks, Nicolas Mhango, wati oyimbira anasokoneza timu yake kuti igonje ndi timu ya Silver Strikers pomwe wati zigoli zoyamba za Silver sizinali zoyenera kukhala zigoli.
Mhango amayankhula izi atatha masewero omwe timuyi yagonja 4-1 pa bwalo la Bingu ndipo timu yake ndi imene inayamba kugoletsa koma Silver inamwetsa zinayi. Iye wati oyimbira anawabalalitsa osewera ake.
"Timu yanga inayamba bwino koma anakhumudwa ndi mmene oyimbira anachitira, chigoli choyamba sichinali penate ndipo chachiwiri sichimayenera kukhalanso chigoli nde zinawafoola osewerawa." Anatero Mhango.
Iye anati anayesetsa kuwauza osewera awo kuti achilimike kuti asewerebe ndikupeza mwayi otsalabe mu ligi pomwe ali pa nambala 14 ndi mapointsi 23 pa masewero 21.