Login with Facebook to post predictions, updates & live scores
"TAKHUTIRA NDI KUFANANA MPHAMVU" - KAUNDA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Oscar Kaunda, wati ndi wokhutira ndi kufanana mphamvu ndi timu ya Bangwe All Stars pomwe wati kubwerera ndi point imodzi ku Blantyre ndi chamuna chomwe.
Iye amayankhula atatha masewero omwe anafanana mphamvu 1-1 pa bwalo la Mpira ndipo wati wakondwa ndi anyamata ake poti anakwanitsa kubwenza chigoli chomwe Bangwe inapeza.
"Ndife okhutira kwambiri ndi mmene masewerowa athera. Tinayamba bwino pomwe tinamenya pagolo kwambiri kuposa Bangwe koma anawapatsa penate komabe tinawalimbikitsa osewera mpaka akwanitsa kupeza chigoli nde kufanana mphamvu ndi zotsatira zabwino koyenda." Anatero Kaunda.
Timuyi tsopano ili pa nambala yachisanu ndi chinayi (9) pomwe ili ndi mapointsi anayi pa masewero atatu omwe yasewera.
MUTUMIZILE KU 0981511741
"TIKUFUNITSITSA CHIPAMBANO KUPOSA CHITIPAYO" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati timu yake ikufunitsitsa kuchita bwino mmasewero awo kusiyana ndi Chitipa United pomwe yati ikufuna kumatolera ma points masewero omwe akusewera.
Iye amayankhula patsogolo pokumana ndi Chitipa United lamulungu pa bwalo la Karonga ndipo wamema masapota awo kufika pa bwaloli kuti adzawapatse mphamvu.
"Ndi masewero ovuta kutengera kuti anzathuwa akuchoka kogonja komabe ifeyo tikufunitsitsa chipambano kuposa iwowo. Mbiri simagwira ntchito awa ndi masewero ena nde masapota abwere tiwapatsanso zosangalatsa." Anatero Kajawa.
Timuyi inayamba ndi kupambana 1-0 mmasewero awo oyamba mu ligi ndipo tsopano Ali pa nambala yachisanu ndi chiwiri (7) ndi mapointsi atatu.
"WE ARE BUILDING A NEW TEAM OF YOUNGSTERS" - KAJAWA
Karonga United coach, Trevor Kajawa, said his players worked according to their plan but struggled because they are new in the league.
He said this after sealing a 1-0 win over Baka City at the Karonga Stadium on Sunday and said his team is being newly built with youngsters hence the struggle.
"It was a good game, we worked according to the plan, in the first half we knew Baka City will come hard so we closed the spaces and in the second half we changed the approach and we got the goal. We struggled because some guys are new in the league, I think if they get used, we will have a good team." Said Kajawa.
The team sits on position 5 after picking their first win and have three points in the league.
NEWS
Karonga United has announced the signing of a 19 year old winger, Obby Raphael Amos from Iponga FC.
The youngster has penned a two year deal with Ingwina as they look to build a strong side ahead of the 2024 season.
The team has made the announcement via their official Facebook page.
Karonga United has announced the signing of Striker, Blessings Mwalilino, who has penned a three year deal with the team
SIGNING:
Karonga United has announced the signing, Kennedy Mwakabaghe, a winger from Iponga Fc.
He has penned a three years contract on Thursday.
NEW SIGNING
Karonga United has also announced the signing of the Extreme FC goalkeeper, Maclean Mwale.
Mwale has penned a two years contract with Ingwina ahead of the 2024 season.
Karonga United has announced the Signing of defender, William Mwalwimba.
Mwalwimba has joined the club as a free agent after being released by Civo United and has signed a two years contract.
"ZIGOLI TANGOWAPATSA MPAKE ZATIVUTA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati anyamata ake sanali bwino kwambiri pomwe amalakwitsa ndipo zigoli zonse angowapatsa a Bangwe All Stars komabe ayesetsa kuti chaka cha mawa adzafikenso ndi mphamvu.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe agonja 3-0 ndi Bangwe All Stars pa bwalo la Mpira lamulungu ndipo wati timu yake sinasewere bwino kwambiri.
"Sitinali bwino anyamata anachotsa chidwi makamaka kumbuyo kwathu mutha kuona kuti tangowapatsa zigoli zija, china tazichinya china penate nde zativuta basi. Tinalibe timu yolimba kwambiri mwina ndi zomwe zimativuta koma chaka cha mawa titolerabe kuti mwina tikhale ndi osewera oti titha kumaliza nawo ligi yonse." Anatero Kajawa.
Kugonjaku kwapangitsa timuyi kuti ituluke mu ndandanda wa matimu asanu ndi atatu (8) pomwe yathera pa nambala 9 ndi mapointsi 38 pa masewero 30 mu ligiyi.
Wolemba: Hastings Wadza Kasonga Jr
"TILIBE PHUMA LILILONSE KOMA BULLETS ILI NALO" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati timu yake ilibe phuma lililonse patsogolo pa masewero awo ndi FCB Nyasa Big Bullets mu ligi ya TNM koma wati Bullets ndi yomwe ili ndi phuma kuti iwine.
Kajawa amayankhula patsogolo pa masewero awo pa bwalo la Karonga lachitatu ndipo wati anyamata ake akudziwa kufunikira kopambana masewerowa kuti athere mu matimu asanu ndi atatu oyamba.
"Tilibe phuma lililonse mwina tikanakhala ndi phuma tikanati mwina tili poti tituluka koma anzathuwa nde ali ndi phuma chifukwa akufuna kutenga ligi nde ifeyo takonzekera, sitimagonjagonja pakhomo nde tionetsetsa kusunga mbiri imeneyi kuti tichite bwino tithere mu Top 8." Anatero Kajawa.
Atakumana mchigawo choyamba, Bullets inapambana 2-0 ku Blantyre. Karonga ili pa nambala 8 ndi mapointsi 37 pa masewero 28 omwe yasewera mu ligiyi.
Players
"TINALI NDI MIPATA YAMBIRI YOTI TIKANATHA KUPAMBANA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati ndi wokondwa kamba koti timu yake yapeza point imodzi pamwamba pa timu ya Silver Strikers ndipo wati ziwathandiza mmasomphenya awo omaliza pabwino.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe afanana mphamvu 0-0 pa bwalo la Karonga ndipo anati anyamata ake anasewera bwino kuposa Silver Strikers.
"Anali masewero abwino kwambiri, kuimitsa timu ngati Silver Strikers ndekuti anyamata achita bwino kwambiri. Tinali ndi mipata yambiri yoti tikanatha kupeza zigoli, Silver inangopeza mpata umodzi mchigawo chachiwiri komabe point imodzi ndi yabwino." Anatero Kajawa.
Iye anati pa masewero atatu omwe atsala nawo ndi FCB Nyasa Big Bullets, Bangwe All Stars komanso Mighty Wakawaka Tigers, ayesetsa kuti achite bwino. Karonga ili pa nambala yachisanu ndi chimodzi ndi mapointsi 37 pa masewero 27.
Mighty mukuru kwiman kwambir kt aneba asatimvutitse
"NZOVUTA KUFOTOKOZA, TAGONJA MOPWETEKA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati timu yake yagonja mmasewero awo omwe amatsogola 2-0 ndi Red Lions kamba koti anyamata ake anatayilira Poona kuti apambana kale.
Kajawa amayankhula izi atatha masewero omwe agonja 3-2 pomwe anagoletsetsa zigoli zitatu mu mphindi zisanu zakumapeto ndipo wati ndi zinthu zovuta kuzimvetsetsa.
"Ndi Zovuta kufotokoza, tagonja tikutsogola 2-0 mpaka anzathu anabweramo, mwina anyamata anatayilira poyesa kuti apambana masewerowa koma zimangofunika kuti tingomalizitsa mpirawu sindikudziwa kuti chachitika ndi chani koma ndi mmene mpira umakhalira." Anatero Kajawa.
Kutsatira kugonjaku, Karonga ikhalabe pa nambala yachisanu ndi chimodzi pomwe ili ndi mapointsi 33 pa masewero 24 omwe yasewera mu ligiyi.
#Tawonga2023
"RED LIONS SI TIMU YOTI YATULUKA KAPENA YOPHWEKA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati wawauza osewera ake kuti asayiphweketse Red Lions ponena kuti akhale masewero ovuta kukumana nayo.
Iye amayankhula izi patsogolo pa masewero awo omwe ali pa bwalo la Karonga lachitatu ndipo wati timu yawo ikufunikira mapointsi onse atatu kuti imalize pabwino mu ligiyi.
"Red Lions si timu yoti yatuluka kapena kuti mwina ikuvutika nde zikakhala zophweka ayi. Tawauza osewera kufunikira kopeza chipambano mmasewerowa ndipo lachitatu tikuyembekeza kuchita bwino." Anatero Kajawa.
Iye wati Nanson Mbewe yekha ndi yemwe sapezeka kamba koti ali ndi makadi achikasu atatu. Karonga ili pa nambala yachisanu ndi chimodzi ndi mapointsi 33 pa masewero 23 mu ligi.
"TIMAFUNA MAPOINTSI 7 KOMA ZAVUTA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati timu yake inayika mulingo kuti ipeze mapointsi okwana asanu ndi awiri (7) pa masewero awo atatu omwe asewera koyenda koma poti zavuta, afuna kuti abwerere ndi anayi.
Iye amayankhula izi lachiwiri patsogolo pa masewero awo ndi Dedza Dynamos ku Dedza ndipo wati masewerowa akhala ovuta poti ali koyenda komanso Dedza ifuna kuzitolera pa kugonja kwawo ndi Bullets koma akufunabe chipambano.
"Tinapanga target kuti tidzatenge mapointsi 7 koma sizinatero pano tatenga imodzi ndipo atsala atatu a mawa, tiyesetsa kuti tiwatenge amenewo kuti tibwerere ndi anayi. Akhala masewero ovuta kwambiri, Dedza tunayichinya mchigawo choyamba koma awa ndi masewero ena komabe anyamata akonzeka." Anatero Kajawa.
Timu ya Karonga ili pa nambala yachisanu ndi chimodzi (6) pomwe ili ndi mapointsi 32 pa masewero 23 omwe yasewera mu ligiyi.
"OYIMBIRA SANAONE ZOLAVULILIDWAZO" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati oyimbira Kondwani Kamwendo, sanalakwitse kuchotsa kalata yofiira ya Katswiri wawo, Allen Chihana, kamba koti analibe umboni okwanira oti katswiriyu analavuliradi osewera wa Civo.
Iye amayankhula izi atatha masewero omwe analepherana 1-1 ndi Civo ndipo masewerowa anaimba kwa pafupifupi mphindi makumi awiri kutsatira Karonga kukana kalatayi kuti ilibe umboni. Iye wati Civo inangomuuza oyimbira zabodza poti katswiriyu amawazunguza.
"Sindikufunapo kuyankhula zambiri koma ndi zoti oyimbira anali zoti sanazione anangouzidwa basi nde ndikuona kuti a Civo anapanga dala chifukwa Allen anali kuti akukwavutitsa kwambiri nde amafuna atuluke koma anali masewero abwino, Civo yasewera bwino mchigawo choyamba ife chachiwiri." Anatero Kajawa.
Timu ya Karonga United ikadali pa nambala yachisanu ndi chimodzi (6) pomwe ili ndi mapointsi 32 pa masewero 23 amene yasewera.
"TINACHITAYA MU CHIGAWO CHACHIWIRI" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati kugonja kwa timu yake ndi timu ya Mighty Mukuru Wanderers mu ligi ya TNM ndi chifukwa choti mu chigawo chachiwiri sanasewere bwino.
Kajawa amayankhula izi atatha masewerowa omwe agonja 2-1 ndipo timuyi imatsogola mchigawo choyamba koma Christopher Kumwembe anamwetsa zigoli ziwiri mu chigawo chachiwiri kuti Manoma apambane. Iye wati mchigawo chachiwiri sanasewere bwino.
"Tagonja inde komabe anyamata asewera bwino, anayesetsa komabe mchigawo chachiwiri zinativuta pomwe mwina amakhutira kuti akutsogola pomwe anakhazikika kumbuyo ngakhale kuti sitinawauze zimenezo. Tivomereze kuti zativuta ndithu." Anatero Kajawa.
Kugonja kumeneko ndi koyamba kwa mphunzitsiyu kutimuyi yomwe ikadali pa nambala yachisanu ndi mapointsi 31 pa masewero 22 mu ligiyi.
"TIKUKUMANA NDI WANDERERS YOKWIYA KOMA SITIKUSAMALA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United, Trevor Kajawa, wati masewero atimu yake ndi Mighty Mukuru Wanderers akhala ovuta kwambiri potengera kuti Wanderers ili yokwiya ndi zotsatira za masewero awo awiri apitawa.
Kajawa amayankhula izi patsogolo pa masewerowa omwe achitikire pa bwalo la Kamuzu lachitatu ndipo iye wati timu yake yakonzeka kukalimbana ndi Manoma mmasewero ovuta kwambiri.
"Ifeyo takonzeka, tikudziwa kuti Wanderers sibwera mophweka chifukwa choti sinachite bwino mmasewero awiri apitawa koma ndi mmene tachitira mmasewero anayi apitawa nafe timu yake ikuonetsa kuti siyophwekanso. Iwo abwera mokwiya koma sitikusamala, tilimbana nawo mpaka titenge 3 points." Anatero Kajawa.
Timu ya Karonga United sinagonjeko chibwerereni Kajawa kutimuyi ndipo ili pa nambala yachisanu ndi mapointsi 32 pa masewero 21 omwe yasewera mu ligiyi.
"NGAKHALE KU MANGALANDE MATIMU AKUMUNSI AMAVUTA" - KAJAWA
Mphunzitsi watimu ya Karonga United wati masewero awo ndi Blue Eagles anali ovuta kwambiri kutengera kuti Eagles ili kumunsi ndipo matimu oterewa amavuta kulikonse.
Mphunzitsiyu amayankhula izi atatha masewero omwe matimuwa afanana mphamvu 0-0 pa bwalo la Karonga ndipo wati timu yake yasewera bwino kwambiri.
"Anali masewero ovuta kwambiri kutengera kuti anzathuwa akuthawa kumunsi kuja nde tinadziwa kuti abwera mwa mphamvu komabe anyamata anayesetsa komabe ngakhale ku England, timu imene ili kumunsi olo ikamasewera ndi Manchester United imavuta." Anatero Kajawa.
Iye wati akufunitsitsa kupeza zipambano zochulukabe kuti akhale pa nambala yabwino ikamatha ligi ya chaka chino. Karonga yaimabe pa nambala yachisanu ndi chimodzi (6) ndi mapointsi 28 pa masewero 21.